Chikhulupiriro
Kodi timadziwa bwanji kuti Yehova amafuna kuti tizikhala ndi chikhulupiriro?
Yoh 3:16, 18; Aga 3:8, 9, 11; Aef 6:16; Ahe 11:6
Onaninso 2Ak 5:7
Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:
Ahe 11:1–12:3—Mtumwi Paulo anafotokoza zokhudza chikhulupiriro komanso zitsanzo za anthu angapo omwe anali ndi chikhulupiriro, kuyambira pa Abele n’kumalizira ndi Yesu Khristu
Yak 2:18-24—Yakobo anafotokoza kuti timasonyeza kuti tili ndi chikhulupiriro mwa zochita zathu ngati mmene Abulahamu anachitira
N’chiyani chingatithandize kuti tilimbitse chikhulupiriro chathu?
Aro 10:9, 10, 17; 1Ak 16:13; Yak 2:17
Onaninso Ahe 3:12-14
Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:
2Mb 20:1-6, 12, 13, 20-23—Adani ataukira anthu a Mulungu, Mfumu Yehosafati anawauza kuti azikhulupirira Yehova ndi aneneri ake kuti zinthu ziwayendere bwino
1Mf 18:41-46—Mneneri Eliya anasonyeza chikhulupiriro poyembekezera moleza mtima kuti Yehova akwaniritse lonjezo lake lakuti adzathetsa chilala chomwe chinatenga nthawi yaitali