Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

Pitani ku mitu ya nkhani

Chikhulupiriro

Chikhulupiriro

Kodi timadziwa bwanji kuti Yehova amafuna kuti tizikhala ndi chikhulupiriro?

Yoh 3:16, 18; Aga 3:8, 9, 11; Aef 6:16; Ahe 11:6

Onaninso 2Ak 5:7

  • Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:

    • Ahe 11:1–12:3​—Mtumwi Paulo anafotokoza zokhudza chikhulupiriro komanso zitsanzo za anthu angapo omwe anali ndi chikhulupiriro, kuyambira pa Abele n’kumalizira ndi Yesu Khristu

    • Yak 2:18-24​—Yakobo anafotokoza kuti timasonyeza kuti tili ndi chikhulupiriro mwa zochita zathu ngati mmene Abulahamu anachitira

N’chiyani chingatithandize kuti tilimbitse chikhulupiriro chathu?

Aro 10:9, 10, 17; 1Ak 16:13; Yak 2:17

Onaninso Ahe 3:12-14

  • Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:

    • 2Mb 20:1-6, 12, 13, 20-23​—Adani ataukira anthu a Mulungu, Mfumu Yehosafati anawauza kuti azikhulupirira Yehova ndi aneneri ake kuti zinthu ziwayendere bwino

    • 1Mf 18:41-46​—Mneneri Eliya anasonyeza chikhulupiriro poyembekezera moleza mtima kuti Yehova akwaniritse lonjezo lake lakuti adzathetsa chilala chomwe chinatenga nthawi yaitali