Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

Pitani ku mitu ya nkhani

Kukhululuka

Kukhululuka

Kodi Yehova ndi wofunitsitsa kukhululuka?

Sl 86:5; Da 9:9; Mik 7:18

Onaninso 2Pe 3:9

  • Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:

    • Sl 78:40, 41; 106:36-46​—Yehova ankakhululukira anthu ake mobwerezabwereza ngakhale kuti zimene ankachitazo zinkamukhumudwitsa

    • Lu 15:11-32​—Yesu anapereka fanizo losonyeza zimene Yehova amachita potikhululukira ndipo anafotokoza za bambo wachifundo yemwe anakhululukira mwana wake pambuyo poti walapa

Kodi Yehova anachita chiyani kuti azitikhululukira machimo?

Yoh 1:29; Aef 1:7; 1Yo 2:1, 2

  • Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:

    • Ahe 9:22-28​—Mtumwi Paulo anafotokoza kuti Khristu anakhetsa magazi ake imene ndi njira yokhayo yomwe imatithandiza kuti tikhululukidwe machimo

    • Chv 7:9, 10, 14, 15​—Mtumwi Yohane anaona m’masomphenya “khamu lalikulu la anthu” omwe anali oyera pamaso pa Mulungu chifukwa chokhulupirira nsembe ya Yesu

Anthu ena akatilakwira, kodi tiyenera kuchita chiyani ngati tikufuna kuti Yehova azitikhululukira?

Mt 6:14, 15; Mko 11:25; Lu 17:3, 4; Yak 2:13

  • Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:

    • Yob 42:7-10​—Yehova asanachotsere Yobu mavuto ake komanso kumudalitsa, anamuuza kuti apempherere anzake atatu omwe ankalankhula zosalimbikitsa aja

    • Mt 18:21-35​—Yesu anafotokoza nkhani yosonyeza kuti ngati tikufuna kuti Yehova atikhululukire, nafenso tizikhululukira anthu ena

N’chifukwa chiyani tifunika kuulula komanso kulapa moona mtima tikachimwa?

Mac 3:19; 26:20; 1Yo 1:8-10

  • Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:

    • Sl 32:1-5; 51:1, 2, 16, 17​—Davide anavutika kwambiri mumtima atachita machimo aakulu kenako analapa moona mtima

    • Yak 5:14-16​—Yakobo ananena kuti ngati tachita tchimo lalikulu, tizifotokozera akulu

Kodi tiyenera kusintha zinthu ziti ngati tikufuna kuti Yehova atikhululukire?

Miy 28:13; Yes 55:7; Aef 4:28

  • Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:

    • 1Mf 21:27-29; 2Mb 18:18-22, 33, 34; 19:1, 2​—Ahabu anamva chisoni Yehova atamuuza kuti amupatsa chilango koma anamuchitira chifundo. Komabe, iye sanasonyeze kudzichepetsa kuti walapa moona mtima, choncho sanamukhululukire ndipo anaphedwa

    • 2Mb 33:1-16​—Ngakhale kuti Manase anachita zoipa zambiri, atalapa Yehova anamukhululukira. Koma pambuyo pake anasintha, anathandiza Aisiraeli kusiya kulambira mafano n’kuyamba kulambira Yehova

Ngati talapa moona mtima, kodi Yehova angatikhululukire kufika pati?

Sl 103:10-14; Yes 1:18; 38:17; Yer 31:34; Mik 7:19

  • Nkhani ya m’Baibulo yomwe ingakuthandizeni:

    • 2Sa 12:13; 24:1; 1Mf 9:4, 5​—Ngakhale kuti Davide anachita machimo aakulu kwambiri, Yehova anamukhululukira atalapa kenako anamutchula kuti ndi munthu wokhulupirika

Kodi Yesu anachita chiyani potengera chitsanzo cha Yehova pa nkhani yokhululukira ena mofunitsitsa?

Sl 86:5; Lu 23:33, 34

  • Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:

    • Mt 26:36, 40, 41​—Yesu atapeza ophunzira ake akugona pa nthawi yomwe iye ankafuna kuti akhale nawo limodzi, anawamvetsa ataona kuti atopa

    • Mt 26:69-75; Lu 24:33, 34; Mac 2:37-41​—Petulo atamukana Yesu katatu kuti sakumudziwa, anamukhululukira atalapa. Kenako, Yesu ataukitsidwa anakaonekera kwa iye ndipo pambuyo pake anamugwiritsa ntchito mwapadera kuti athandize mipingo

Kodi timadziwa bwanji kuti si machimo onse amene Yehova amakhululuka?

Mt 12:31; Ahe 10:26, 27; 1Yo 5:16, 17

  • Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:

    • Mt 23:29-33​—Yesu anachenjeza alembi ndi Afarisi kuti adzaweruzidwa mwa kuponyedwa m’Gehena, kapena kuti chiwonongeko chotheratu

    • Yoh 17:12; Mko 14:21​—Yesu anatchula Yudasi Isikarioti kuti “mwana wa chiwonongeko” ndipo ananena kuti zikanakhala bwino akanapanda kubadwa

N’chiyani chimene chingatithandize kuti tizikhululukira ena?