Mtima
Kodi timadziwa bwanji kuti Baibulo likamagwiritsa ntchito mawu akuti “mtima,” nthawi zambiri limatanthauza umunthu wathu wamkati, kuphatikizapo maganizo, zolinga, makhalidwe komanso mmene tikumvera?
Sl 49:3; Miy 16:9; Lu 5:22; Mac 2:26
-
Nkhani ya m’Baibulo yomwe ingakuthandizeni:
-
Lu 9:46-48—Yesu anadzudzula atumwi ake ataona kuti anali ndi mtima wodziona ngati apamwamba
-
N’chifukwa chiyani timafunika kuteteza mtima wathu?
-
Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:
-
Ge 6:5-7—Kuipa kwa mtima wa anthu kunachititsa kuti azichita zachiwawa ndipo chifukwa cha zimenezi, Mulungu anabweretsa Chigumula padziko
-
1Mf 11:1-10—Mfumu Solomo analephera kuteteza mtima wake ndipo anakwatira akazi achilendo, omwe anamuchititsa kuti asiye kutumikira Mulungu wake ndi mtima wonse
-
Mko 7:18-23—Yesu anafotokoza kuti maganizo oipa amayambira mumtima ndipo angachititse kuti tichite zinthu zomwe Mulungu amadana nazo
-
Kodi tingateteze bwanji mtima wathu?
Sl 19:14; Miy 3:3-6; Lu 21:34; Afi 4:8
Onaninso Eza 7:8-10; Sl 119:11
-
Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:
-
Aef 6:14-18; 1At 5:8—Pofotokoza zida za nkhondo yauzimu, mtumwi Paulo ananena kuti chilungamo, chikhulupiriro komanso chikondi zimateteza mtima wathu wophiphiritsa mofanana ndi mmene chodzitetezera pachifuwa chimatetezera mtima weniweni
-
Kodi tingadziwe bwanji kuti mtima wathu wophiphiritsa uli ndi vuto?
Onaninso Miy 6:12-14
-
Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:
-
2Mb 25:1, 2, 17-27—Pa nthawi ina Mfumu Amaziya ankachita zoyenera pamaso pa Mulungu koma sankakonda Yehova ndi mtima wonse. Iye anayamba mtima wodzikuza n’kusiya kutsatira Yehova ndipo pamapeto pake anaphedwa
-
Mt 7:17-20—Yesu ananena kuti tikakhala ndi mtima woipa tingamachitenso zinthu zoipa
-
N’chifukwa chiyani tiyenera kukhala ndi mtima wabwino? Nanga tingatani kuti zimenezi zitheke?
Onaninso Sl 119:97, 104; Aro 12:9-16; 1Ti 1:5
-
Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:
-
2Mf 20:1-6—Mfumu Hezekiya anali wokhulupirika ndipo ankatumikira Yehova ndi mtima wonse. Choncho atadwala anapempha Yehova kuti amuthandize
-
Mt 21:28-32—Yesu ananena fanizo losonyeza kuti zimene zili mumtima mwa munthu zimadziwika ndi zimene amachita kuposa zimene wanena kuti adzachita
-
N’chifukwa chiyani timatonthozedwa tikadziwa kuti Yehova amaona zomwe zili mumtima mwathu?
Onaninso 1Sa 2:3
-
Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:
-
1Sa 16:1-13—Mneneri Samueli anazindikira kuti kwa Yehova, chofunika si mmene munthu amaonekera koma mtima wake
-
2Mb 6:28-31—Pemphero la Mfumu Solomo lotsegulira kachisi wa Yehova, linasonyeza kuti Mulungu amadziwa bwino zomwe zili mumtima wathu, ndipo iye amatisamalira potengera zomwe amadziwa zokhudza ifeyo
-