Kudzichepetsa
Kodi Yehova amawaona bwanji anthu odzichepetsa komanso odzikuza?
Sl 138:6; Miy 15:25; 16:18, 19; 22:4; 1Pe 5:5
Onaninso Miy 29:23; Yes 2:11, 12
-
Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:
-
2Mb 26:3-5, 16-21—Mfumu Uziya anayamba kudzikuza ndipo anasiya kutsatira Chilamulo cha Mulungu. Atapatsidwa malangizo anakwiya ndipo Mulungu anamukantha ndi khate
-
Lu 18:9-14—Yesu ananena fanizo losonyeza mmene Yehova amaonera mapemphero a anthu odzikuza ndi odzichepetsa
-
Kodi Yehova amatani anthu odzichepetsa akalapa mochokera pansi pa mtima?
-
Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:
-
2Mb 12:5-7—Mfumu Rehobowamu ndi akalonga a Yuda anadzichepetsa pamaso pa Yehova ndipo Yehova sanawalange
-
2Mb 32:24-26—Hezekiya yemwe anali mfumu yabwino anayamba kudzikuza koma Yehova anamukhululukira atadzichepetsa
-
Kodi kukhala odzichepetsa kungatithandize bwanji?
Aef 4:1, 2; Afi 2:3; Akl 3:12, 13
-
Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:
-
Ge 33:3, 4—Esau anakwiyira kwambiri Yakobo koma Yakobo anasonyeza kudzichepetsa kwakukulu popita kukakumana naye ndipo zimenezi zinathandiza kuti pakati pawo pakhale mtendere
-
Owe 8:1-3—Woweruza Gidiyoni anauza amuna a ku Efuraimu kuti ndi apamwamba kuposa iyeyo ndipo zimenezi zinathandiza kuti mkwiyo wawo uthe
-
Kodi Yesu Khristu anaphunzitsa bwanji kuti kukhala odzichepetsa n’kofunika kwambiri?
Mt 18:1-5; 23:11, 12; Mko 10:41-45
-
Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:
-
Yes 53:7; Afi 2:7, 8—Mogwirizana ndi zimene aneneri ananeneratu, Yesu anali wodzichepetsa ndipo anali wofunitsitsa kubwera padziko ndiponso kufa imfa yochititsa manyazi komanso yowawa kwambiri
-
Lu 14:7-11—Yesu anafotokoza nkhani yokhudza kukhala pamalo olemekezeka kuphwando pofuna kutithandiza kuona ubwino wa kudzichepetsa
-
Yoh 13:3-17—Yesu anasonyeza otsatira ake chitsanzo chabwino cha kudzichepetsa posambitsa mapazi a atumwi ake
-
Kodi kuona ena komanso ifeyo mmene Yehova amationera kungatithandize bwanji kukhala odzichepetsa?
N’chifukwa chiyani kudzichepetsa kwabodza n’kopanda phindu?