Kumvera
Kodi kumvera kuli ndi ubwino wotani?
Eks 19:5; De 10:12, 13; Mla 12:13; Yak 1:22
-
Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:
-
1Sa 15:17-23—Mneneri Samueli anadzudzula Mfumu Sauli chifukwa chosamvera Yehova; kenako Samueli akumuuza mwamphamvu za kufunika komvera
-
Ahe 5:7-10—Ngakhale kuti nthawi zonse Yesu ankamvera Atate wake, ali padzikoli anaphunzira kumvera pa nthawi imene anthu ankamuzunza
-
Kodi Mkhristu ayenera kuchita chiyani ngati akuluakulu a boma atamuuza kuti asamvere Mulungu?
-
Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:
-
Da 3:13-18—Aheberi atatu anakana kugwadira fano limene Mfumu Nebukadinezara inaimika, ngakhale kuti kuchita zimenezi kunaika moyo wawo pangozi
-
Mt 22:15-22—Yesu anafotokoza kuti otsatira ake amamvera maboma a anthu koma samamvera mabomawo ngati akuwauza kuchita zinthu zosemphana ndi zimene Yehova Mulungu amafuna
-
Mac 4:18-31—Atumwi sanasiye kulalikira ngakhale kuti olamulira anawaletsa
-
Kodi tiyenera kuchita chiyani kuti tisasiye kumvera Yehova?
Onaninso Sl 119:11, 112; Aro 6:17
-
Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:
-
Eza 7:7-10—Ezara anali wansembe wokhulupirika ndipo anakonzekeretsa mtima wake kuti akhale chitsanzo chabwino pa nkhani yomvera Chilamulo cha Yehova komanso kuphunzitsa ena
-
Yoh 14:31—Yesu anafotokoza chifukwa chake amachita zinthu ndendende mmene Atate wake anamutumira
-
N’chifukwa chiyani tiyenera kumvera Yehova ndi Yesu?
Kodi kumvera kumasonyeza bwanji kuti tili ndi chikhulupiriro?
Aro 1:5; 10:16, 17; Yak 2:20-23
Onaninso De 9:23
-
Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:
-
Ge 6:9-22; Ahe 11:7—Nowa anasonyeza chikhulupiriro pomanga chingalawa ndendende mogwirizana ndi mmene Yehova anamulamulira ndipo “anachitadi zomwezo”
-
Ahe 11:8, 9, 17—Abulahamu anasonyeza chikhulupiriro pomvera Yehova atamuuza kuti achoke ku Uri, komanso atamuuza kuti apereke mwana wake nsembe
-
Kodi Yehova amadalitsa bwanji anthu omvera?
-
Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:
-
Le 26:3-6—Yehova analonjeza kuti adzadalitsa ndi kusamalira anthu amene amamumvera
-
Nu 13:30, 31; 14:22-24—Kalebe anali womvera ndipo Yehova anamudalitsa
-
Kodi kusamvera kumabweretsa mavuto otani?
-
Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:
-
Ge 2:16, 17; 3:17-19—Adamu ndi Hava anataya mwayi wokhala ndi moyo wangwiro kwamuyaya, m’Paradaiso, chifukwa sanamvere Yehova Mulungu
-
De 18:18, 19; Mac 3:12, 18, 22, 23—Yehova analosera kuti kudzabwera mneneri wamkulu kuposa Mose komanso kuti amene sadzamvera mneneriyu adzalandira chilango
-
Yuda 6, 7—Angelo opanduka komanso anthu osamvera a ku Sodomu ndi Gomora anaputa mkwiyo wa Yehova
-
N’chifukwa chiyani tiyenera kumvera Yesu Khristu?
-
Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:
-
Yoh 12:46-48; 14:24—Yesu anafotokoza kuti tikapanda kumvera mawu ake, tidzalandira chilango m’tsogolo
-
N’chifukwa chiyani Akhristu ayenera kumvera akulu mumpingo?
N’chifukwa chiyani mkazi wa Chikhristu ayenera kumvera mwamuna wake?
N’chifukwa chiyani ana ayenera kumvera makolo awo?
-
Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:
-
Ge 37:3, 4, 8, 11-13, 18—Yosefe ali mwana ankamvera bambo ake ndipo anapita kukaona azichimwene ake ngakhale kuti ankadana naye
-
Lu 2:51—Yesu anapitirizabe kumvera Yosefe ndi Mariya ngakhale kuti iye anali wangwiro koma makolo akewo sanali angwiro
-
N’chifukwa chiyani ndi nzeru kumamvera mabwana athu ngakhale pamene anthu ena sakutiona?
N’chifukwa chiyani Akhristu amamvera maboma?