Nzeru
Kodi timafunika kuchita chiyani kuti tikhale ndi nzeru zenizeni?
Kodi tingapeze kuti nzeru zenizeni?
Kodi ndi zoyenera kupemphera kwa Mulungu kuti atipatse nzeru?
-
Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:
-
2Mb 1:8-12—Mfumu Solomo ali wamng’ono anapemphera kuti akhale ndi nzeru n’cholinga choti azilamulira bwino Isiraeli ndipo Yehova anamupatsa nzeru
-
Miy 2:1-5—Baibulo limayerekezera nzeru, kumvetsa zinthu komanso kuzindikira ndi chuma chobisika chimene timafunika kuchifufuza ndipo Yehova amathandiza anthu omwe amachifunafuna ndi mtima wawo wonse
-
Kodi Yehova amapereka bwanji nzeru?
Yes 11:2; 1Ak 1:24, 30; 2:13; Aef 1:17; Akl 2:2, 3
-
Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:
-
Miy 8:1-3, 22-31—Nzeru imafotokozedwa ngati munthu ndipo zimenezi zimatikumbutsa za Mwana wa Mulungu yemwe anali woyambirira kulengedwa zinthu zina zonse zisanalengedwe
-
Mt 13:51-54—Anthu ambiri omwe ankamvetsera zimene Yesu ankaphunzitsa, anadabwa kwambiri kuti zikutheka bwanji kuti munthu yemwe anakula akumuona akhale ndi nzeru zochuluka choncho
-
Kodi timadziwa bwanji kuti tili ndi nzeru zochokera kwa Mulungu?
Sl 111:10; Mla 8:1; Yak 3:13-17
Onaninso Sl 107:43; Miy 1:1-5
Kodi nzeru zimatithandiza komanso kutiteteza bwanji?
Onaninso Miy 7:2-5; Mla 7:12
Kodi nzeru zochokera kwa Mulungu ndi zothandiza bwanji?
Onaninso Yob 28:18
-
Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:
-
Yob 28:12, 15-19—Ngakhale kuti Yobu anavutika kwambiri, iye anayamikira nzeru zochokera kwa Mulungu
-
Sl 19:7-9—Mfumu Davide ananena kuti chilamulo cha Yehova ndiponso zikumbutso zake zimapatsa nzeru munthu wosadziwa zinthu
-
N’chifukwa chiyani n’zoopsa kutsatira nzeru za anthu am’dzikoli omwe amanyalanyaza Mulungu?