Onani zimene zilipo

Onani nkhani zake

KUBWELELAKO

Yohane 7:3-5; 1 Akor. 15:3, 4, 7

PHUNZILO 8

Kuleza Mtima

Kuleza Mtima

Mfundo Yaikulu: “Cikondi n’coleza mtima.”—1 Akor. 13:4.

Mmene Yesu Anaonetsela Khalidwe Limeneli

1. Tambani VIDIYO, kapena ŵelengani Yohane 7:3-5 na 1 Akorinto 15:3, 4, 7. Kenaka ganizilani pa mafunso otsatilawa:

  1.    Kodi poyamba abale a Yesu anacita motani atamva uthenga wake?

  2.   N’ciyani cionetsa kuti Yesu sanataye mtima pothandiza m’bale wake Yakobo?

Tiphunzilaponji kwa Yesu?

2. Tizikhala oleza mtima cifukwa anthu ena amatenga nthawi yotalikilapo kuti alabadile uthenga wabwino.

Tengelani Citsanzo ca Yesu

3. Yesani njila ina. Ngati poyamba munthu wakana phunzilo la Baibo, musamuumilize. Pa nthawi yoyenela, muonetseni mavidiyo kapena nkhani zina zomuthandiza kudziŵa mmene phunzilo la Baibo limacitikila, komanso mmene iye angapindulile.

4. Musayelekezele anthu. Munthu aliyense ni wosiyana. Ngati wina m’banja, kapena munthu pa ulendo wobwelelako azengeleza kuphunzila Baibo, kapena kuvolemeleza mfundo inayake ya m’Baibo, ganizilani cingakhale cifukwa cake. Kodi pali zimene amakhulupilila zomwe n’zofunika kwambili kwa iye? Kodi n’cifukwa ca cipembedzo cake? Kodi n’kutheka acibale ake, kapena maneba ake, ni amene amamuopseza? M’patseni nthawi yoti aganizilepo pa mfundo zimene mwamuuzapo, kutinso aone phindu la zimene Baibo imanena.

5. M’pempheleleni munthu wacidwi. Pemphani Yehova akuthandizeni kukhala wacidalilo komabe wosamala. M’pempheninso akuthandizeni kuzindikila pamene muyenela kungomusiya munthu wopanda cidwi ceniceni.—1 Akor. 9:26.

ONANINSO MALEMBA AWA

Maliko 4:26-28; 1 Akor. 3:5-9; 2 Pet. 3:9