KUPANGA OPHUNZILA
PHUNZILO 10
Kudzipeleka pa Nchitoyi
Mfundo Yaikulu: “Tinali okonzeka kukupatsani uthenga wabwino wa Mulungu. Ndipotu osati uthenga wokha ayi, komanso miyoyo yathu yeniyeniyo, cifukwa tinakukondani kwambili.”—1 Ates. 2:8.
Mmene Yesu Anacitila Zimenezi
1. Tambani VIDIYO, kapena ŵelengani Yohane 3:1, 2. Kenaka ganizilani pa mafunso otsatilawa:
Tiphunzilaponji kwa Yesu?
2. Cifukwa timakonda anthu, timadzipeleka kuti tiwathandize kukhala ophunzila.
Tengelani Citsanzo ca Yesu
3. Muziphunzila pa nthawi na malo okomela wophunzila Baibo wanu. Iye angasankhe tsiku lakuti-lakuti pa mlungu, kapenanso nthawi yakuti-yakuti. Kodi angakonde kumaphunzilila ku nchito kwake, ku nyumba kwake, kapena pa malo a anthu onse? Monga kungathekele, sinthilani ku nthawi, tsiku, na malo omwe angam’komele.
4. Musamalumphe-lumphe kuphunzila. Ngati simudzakhalapo, musalumphe mlungu umenewo. Ganizilani izi m’malo mwake:
5. Pemphani thandizo kwa Yehova. Pemphani Yehova kuti akuthandizeni kukhalabe wodzipeleka pa kuthandiza wophunzila wanu, ngakhale kuti amaphonya-phonya kuphunzila, kapena amacedwa kugwilitsa nchito zimene mukuphunzila. (Afil. 2:13) N’kutheka kuti wophunzila wanu ali na makhalidwe abwino ambili; muzim’pemphelela kuti awakulitse makhalidwe amenewo.
ONANINSO MALEMBA AWA
Miy. 3:27; Mac. 20:35; 2 Akor. 12:15