KUPHUNZITSA ANTHU
PHUNZIRO 12
Kulangiza Molimba Mtima
Mfundo yaikulu: “Mafuta ndi zofukiza zonunkhira n’zimene zimasangalatsa mtima. Chimodzimodzinso kukhala ndi mnzako wabwino amene amakupatsa malangizo mosapita m’mbali.”—Miy. 27:9.
Zomwe Yesu Anachita
1. Onerani VIDIYO, kapena werengani Maliko 10:17-22. Kenako kambiranani mafunso otsatirawa:
Zomwe Tikuphunzira kwa Yesu
2. Kuti wophunzira wathu apite patsogolo mwauzimu, tiyenera kumulankhula mwachikondi koma mosabisa mawu.
Zomwe Mungachite Potsanzira Yesu
3. Muzimuthandiza kukhala ndi zolinga komanso mmene angazikwaniritsire.
-
Muzigwiritsa ntchito mbali yakuti “Zolinga,” m’buku la Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale.
-
Muzimuthandiza kudziwa zomwe angachite kuti akwaniritse zolinga zing’onozing’ono komanso zikuluzikulu.
4. Muzizindikira zomwe zingamulepheretse kupita patsogolo, n’kumuthandiza.
-
-
‘N’chiyani chomwe chingakhale kuti chikumulepheretsa kupita patsogolo kuti abatizidwe?’
-
Ndingatani kuti ndimuthandize?
-
-
Muzipempha Yehova kuti akuthandizeni kulankhula mwachikondi komanso mosabisa mawu pothandiza wophunzira wanu.
5. Muzisiya kuphunzira naye ngati sakupita patsogolo.
-
Dzifunseni mafunso awa kuti mudziwe ngati phunzirolo likupitadi patsogolo kapena ayi:
-
‘Kodi amagwiritsa ntchito zomwe amaphunzira?’
-
‘Kodi amapezeka pamisonkhano komanso kuuza ena zokhudza choonadi?’
-
‘Popeza waphunzira kwa nthawi yotalikirapo, kodi akufuna kukhala wa Mboni za Yehova?’
-
-
Ngati wophunzira Baibulo sakupita patsogolo:
-
Mufunseni chimene chikumulepheretsa kuti asapite patsogolo.
-
Muuzeni mokoma mtima chifukwa chake simungapitirize kuphunzira naye.
-
Muuzeni zomwe angachite ngati atadzafunanso kupitiriza kuphunzira.
-