Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

Pitani ku mitu ya nkhani

Kodi Kubadwa Mwatsopano N’kofunika Motani?

Kodi Kubadwa Mwatsopano N’kofunika Motani?

Kodi Kubadwa Mwatsopano N’kofunika Motani?

POKAMBIRANA ndi Nikodemo, Yesu anatsindika mfundo yakuti kubadwa mwatsopano, kapena kuti kubadwanso, n’kofunika kwambiri. Kodi iye anasonyeza motani zimenezi?

Taonani mmene Yesu anasonyezera kufunika kobadwa mwatsopano pokambirana ndi Nikodemo. Iye anati: “Munthu sangathe kuona ufumu wa Mulungu atapanda kubadwanso.” (Yohane 3:3) Mawu akuti “sangathe” ndiponso “atapanda” akusonyeza kufunika kobadwa mwatsopano. Mwachitsanzo, munthu atanena kuti, “Dzuwa litapanda kutuluka, kunja sikungache,” akutanthauza kuti dzuwa n’lofunika kwambiri kuti kunja kuche. Mofanana ndi zimenezi, Yesu ananena kuti kubadwanso n’kofunika kwambiri kuti munthu aone Ufumu wa Mulungu.

Pomalizira, Yesu ananena mawu otsatirawa pofuna kutsindika mfundoyi. Iye anati: “Anthu inu muyenera kubadwanso.” (Yohane 3:7) Choncho, malinga ndi zimene Yesu ananenazi, kuti munthu ‘akalowe mu Ufumu wa Mulungu,’ ayenera kubadwanso.​—Yohane 3:5.

Yesu anaona kuti kubadwa mwatsopano n’kofunika kwambiri. Choncho, Akhristu ayenera kuonetsetsa kuti nkhani imeneyi akuyimvetsa bwino. Mwachitsanzo, kodi mukuganiza kuti Mkhristu angasankhe yekha kuti abadwenso?

[Mawu Otsindika patsamba 5]

“Dzuwa litapanda kutuluka, kunja sikungache”