Mulungu Walonjeza Kuti Matenda a Maganizo Adzathelatu
Kupitila m’Baibo, Mulungu amapeleka malangizo na cilimbikitso kwa anthu amene ali na matenda ovutika maganizo.
Koma iye wacita zambili kuposa pamenepa. Walonjeza kuti adzacotselatu zonse zimene zimabweletsa matenda a maganizo.
Mulungu akadzakwanilitsa lonjezo limeneli, sipadzakhalanso kuwawidwa mtima, kupanikizika maganizo, komanso zinthu zoipa zakale “sizidzakumbukilidwanso, ndipo sizidzabwelanso mumtima.”—Yesaya 65:17.
Mboni za Yehova ni zokonzeka kukuthandizani kudziŵa kuti ni liti komanso ni motani mmene Mulungu adzakwanilitsila lonjezo lolimbikitsa limeneli.