Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

Pitani ku mitu ya nkhani

Kulalikira ndi Kuphunzitsa Padziko Lonse

Kulalikira ndi Kuphunzitsa Padziko Lonse

 PADZIKO LONSE

  • MAYIKO 239

  • OFALITSA 7,965,954

  • MAOLA ONSE AMENE TINATHERA MU UTUMIKI WAKUMUNDA 1,841,180,235

  • MAPHUNZIRO A BAIBULO 9,254,963

M'CHIGAWO ICHI

Africa

Anthu ambiri ku Africa akuphunzira Baibulo ndipo akusintha kwambiri makhalidwe awo. Werengani za munthu amene anasiya kumwa mowa mwauchidakwa komanso kusuta ndudu 60 patsiku.

North ndi South America

Nkhanizi zikusonyeza kuti ntchito yolalikira imayenda bwino ngati timathandiza ena komanso timalalikira ngakhale kuti timatsutsidwa.

Asia ndi Middle East

Khama limene abale akusonyeza pa ntchito yolalikira likubala zipatso. Werengani nkhaniyi kuti muone zimene munthu wina anachita kuti athandize munthu yemwe ndi wosamva, wosaona komanso wosalankhula, kuti adziwe zoti Mulungu amamukonda.

Europe

Anthu amadana ndi Mboni chifukwa cha zabodza zomwe anauzidwa. Werengani nkhaniyi kuti mudziwe mmene pulogalamu ya pawailesi inathandizira anthu kuti asiye kudana ndi Mboni za Yehova.

Oceania

Kulemba makalata ndi njira ina yomwe choonadi cha m’Baibulo chikufalitsidwira mumzinda wa Christchurch ku New Zealand. N’chifukwa chiyani ena amatchula makalatawa kuti “Makalata Ochokera kwa Mulungu?”