Kodi Mungatani Kuti ‘Mulungu Apitirize Kukukondani’?

Bukuli likuthandizani kuti mupitirize kugwiritsa ntchito mfundo za m’Baibulo pa moyo wanu zimene zingachitse kuti Mulungu apitirize kukukondani.

Kalata Yochokera ku Bungwe Lolamulira

Bungwe Lolamulira la Mboni za Yehova likulimbikitsa onse omwe amakonda Yehova kuti azitsanzira chitsanzo cha Yesu yemwe ankachita zinthu zomwe zinachititsa kuti Atate ake azimukondabe.

MUTU 1

Zimene “Kukonda Mulungu Kumatanthauza”

Baibulo limafotokoza m’mawu aafupi mmene tingachitire zimenezi.

MUTU 2

Kodi Mungatani Kuti Mukhalebe ndi Chikumbumtima Chabwino?

Kodi zingatheke munthu kukhala ndi chikumbumtima chimene sichikumutsutsa koma chili chodetsedwa pamaso pa Mulungu?

MUTU 3

Muzikonda Anthu Amene Mulungu Amawakonda

Yehova amasankha bwino anthu amene angakhale anzake, ifenso tichita chimodzimodzi.

MUTU 4

Kodi N’chifukwa Chiyani Tiyenera Kulemekeza Ulamuliro?

TMalemba amasonyeza njira zitatu zimene Yehova amafuna kuti tizitsatira posonyeza kuti timamvera amene akutilamulira.

MUTU 5

Kodi Tingatani Kuti Tikhale Osiyana ndi Dzikoli?

Mawu a Mulungu amafotokoza njira 5 zimene tingasonyezere kuti ndife osiyana ndi dzikoli.

MUTU 6

Kodi Mungasankhe Bwanji Zosangalatsa Zabwino?

Mafunso atatu omwe angakuthandizeni kuti muzisankha mwanzeru.

MUTU 7

Kodi Mumalemekeza Moyo Ngati Mmene Mulungu Amachitira?

Kulemekeza moyo kumatanthauza zambiri osati kungopewa kupha munthu

MUTU 8

Mulungu Amakonda Anthu Oyera

Baibulo lingakuthandizeni kupewa makhalidwe omwe angapangitse kuti musakhale oyera pamaso pa Mulungu.

MUTU 9

“Thawani Dama”

Chaka chilichonse Akhristu ambiri masauzande ambiri amachita chiwerewere. Kodi inuyo mungatani kuti musagwere mumsampha umenewu?

MUTU 10

Ukwati Ndi Mphatso Yochokera Kwa Mulungu Wachikondi

Kodi mungatani kuti banja lanu lizidzayenda bwino? Ngati muli kale pabanja, kodi, kodi mungatani kuti likhalebe mpaka kalekale?

MUTU 11

“Ukwati Ukhale Wolemekezeka”

Pali mafunso 6 omwe angakuthandize kudzifufuza komanso kuti banja lanu liziyenda bwino.

MUTU 12

Muzilankhula Mawu “Olimbikitsa”

Zimene mumalankhula zikhoza kulimbikitsa ena kapena kuwafooketsa. Phunzirani kugwiritsa ntchito bwino mphatso ya kulankhula ngati mmene Yehova amafunira.

MUTU 13

Zikondwerero Zimene Mulungu Amadana Nazo

Zikondwerero komanso miyambo ina yomwe imaoneka ngati ndi yolemekeza Mulungu amanyansidwa nayo.

MUTU 14

Chitani Zinthu Zonse Moona Mtima

Kuti mukwanitse kuchita zinthu moona mtima ndi ena pali pali choyamba chimene muyenera kuchita.

MUTU 15

Sangalalani Chifukwa Chogwira Ntchito Mwakhama

Mayankho a mafunso 5 angakuthandizeni kudziwa ngati ndi zoyenera kulowa ntchito inayake.

MUTU 16

Tsutsani Mdyerekezi ndi Njira Zake

Timadziwa kuti Satana ali ndi mphamvu koma timapewa kuchita naye mantha kwambiri. Chifukwa chiyani?

MUTU 17

‘Dzilimbitseni Pamaziko a Chikhulupiriro Chanu Choyera Kopambana’

TPali zinthu zitatu zimene zingakuthandizeni kuti chikhulupirire chanu chilimbe zomwe zingathandize kuti Mulungu apitirize kukukondani.

ZAKUMAPETO

Mmene Tiyenera Kuchitira ndi Munthu Wochotsedwa

Kodi tifunikadi kumapeweratu anthu ochotsedwa?

ZAKUMAPETO

Kodi Mlongo Ayenera Kuvala Chinachake Kumutu pa Zochitika Ziti, Ndipo N’chifukwa Chiyani?

Baibulo limanena zinthu zitatu zimene mungaziganizire kuti mudziwe ngati mukufunika kumanga chinachake kumutu.

ZAKUMAPETO

Kuchitira Sailuti Mbendera, Kuvota Ndiponso Kugwira Ntchito Zosakhudzana ndi Usilikali

kodi ndi mfundo ziti za m’Malemba zimene zingatithandize kuti tikhale ndi chikumbumtima chabwino pankhani zimenezi?

ZAKUMAPETO

Tizigawo ta Magazi ndi Njira Zopangira Opaleshoni

Kungochita zinthu zochepa chabe mukhoza kuthana ndi mavuto okhudza chithandizo cha chipatala.

ZAKUMAPETO

Mungathe Kuthetsa Vuto Loseweretsa Maliseche

Kodi mungathane bwanji ndi khalidwe loipa limeneli?

ZAKUMAPETO

Zimene Baibulo Limanena pa Nkhani Yothetsa Banja ndi Kupatukana

Kodi Baibulo limati munthu amene banja lake linatha angakhale ndi ufulu wokwatiwa kapena wokwatiranso panthawi iti?

ZAKUMAPETO

Kuthetsa Kusamvana pa Nkhani za Bizinezi

Kodi ndi zoyenera kuti Mkhristu asumire Mkhristu mnzake kukhoti?