Citani Khama pa Kuŵelenga na Kuphunzitsa

Kabuku kano kanakonzedwa kuti kakuthandizeni kunola maluso anu a kuŵelenga, kulankhula, komanso kuphunzitsa.

Kalata Yocokela ku Bungwe Lolamulila

Timalalikila uthenga wofunika kwambili kwa anthu kuposa wina uliwonse.

PHUNZILO 1

Mawu Oyamba Ogwila Mtima

Mawu oyamba ogwila mtima afunika kukwanilitsa zolinga ziŵili.

PHUNZILO 2

Kukambilana Mwacibadwa

Kukambilana mwacibadwa kumamasula omvela anu, komanso kumawathandiza kulabadila uthenga wanu.

PHUNZILO 3

Gwilitsilani Nchito Mafunso

Mafunso aluso angakuthandizeni kuwakopa cidwi omvela anu, na kugogomeza mfundo zofunika.

PHUNZILO 4

Kachulidwe ka Malemba Koyenela

Onani mmene mungakonzekeletsele maganizo a omvela anu musanaŵelenge lemba.

PHUNZILO 5

Kuŵelenga Bwino

Kuŵelenga bwino ni mbali yofunika kwambili pothandiza ena kudziŵa za Yehova.

PHUNZILO 6

Kumveketsa Bwino Cifukwa Coŵelengela Lemba

Thandizani omvela anu kuona bwino-bwino kugwilizana kwa lemba imene mwaŵelenga na mfundo imene mukufotokoza.

PHUNZILO 7

Kukamba Zoona Zokha-Zokha Komanso Zokhutilitsa

Kukamba maumboni a zoona komanso okhulutilitsa, kumathandiza omvela anu kukhutila na zimene mukukamba.

PHUNZILO 8

Mafanizo Ophunzitsadi Kanthu

Phunzitsani mwaluso pogwilitsila nchito mafanizo osavuta kumva kwa omvela anu, komanso kumveketsa mfundo zofunika.

PHUNZILO 9

Kuseŵenzetsa Bwino Zitsanzo Zooneka

Seŵenzetsani zitsanzo zooneka kuti mukhomeleze kwambili mfundo m’maganizo mwa omvela anu.

PHUNZILO 10

Kusintha-sinthako Mawu

Muzisiyanitsa liŵilo la mau anu, kamvekedwe kake, komanso mphamvu yake, kuti mukhudze mtima omvela anu, na kuwalimbikitsa kucitapo kanthu.

PHUNZILO 11

Kukamba Mwaumoyo

Kukamba mwaumoyo kumaonetsa mmene mukumvelela, komanso kumakuthandizani kukopa cidwi ca omvela anu.

PHUNZILO 12

Mzimu Waubwenzi na Cifundo

Ngati mulankhula na mzimu woyenelela, mumaonetsa kuti mumawaganizila omvela anu.

PHUNZILO 13

Kumveketsa Phindu ya Nkhani

Thandizani omvela anu kumvetsa mmene nkhani yanu ikukhudzila umoyo wawo. Komanso afotokozeleni mocitila nazo zimene aphunzila.

PHUNZILO 14

Kumveketsa Bwino Mfundo Zazikulu

Thandizani omvela anu kukutsatilani m’nkhani yanu. Onetsani bwino mmene mfundo yaikulu iliyonse ikugwilizanila na colinga canu, komanso na mutu wa nkhani.

PHUNZILO 15

Kukamba Motsimikiza

Kambani motsimikiza. Onetsani kuti mumakhulupilila kuti zimene mukamba n’zofunika ngako.

PHUNZILO 16

Khalani Wolimbikitsa Komanso Wotsitsimula

Kambani molimbikitsa osati mosuliza. Lunjikitsani nkhani yanu ku mfundo zotsitsimula za m’Mawu a Mulungu.

PHUNZILO 17

Muzikamba Zosavuta Kumvetsa

Thandizani omvela anu kumvetsa zimene mukukamba. Mveketsani mfundo zofunika momveka bwino.

PHUNZILO 18

Nkhani Yophunzitsadi Kanthu Omvela

Kambani mwa njila yopangitsa omvela anu kuganizilapo pa nkhaniyo, na kuwathandiza kuphunzilapodi kanthu.

PHUNZILO 19

Yesetsani Kuwafika pa Mtima Omvela

Limbikitsani omvela anu kukonda Mulungu, na Mawu ake Baibo.

PHUNZILO 20

Mawu Otsiliza Ogwila Mtima

Mawu otsiliza ogwila mtima, adzathandiza omvela anu kuona ubwino wa zimene aphunzila kuti akazigwilitsile nchito.

Lembani Mmene Mwapitila Patsogolo

Lembani mmene mwapitila patsogolo kuti munole maluso anu a kuŵelenga na kuphunzitsa.