Yobu Sanalole Kuti Maganizo Olakwika Amusokoneze
Satana amanena zinthu zabodza pofuna kufooketsa atumiki a Yehova masiku ano. Taonani mfundo zopezeka m’buku la Yobu, zosonyeza kusiyana pakati pa mabodza a Satana ndi mmene Yehova amawonera atumiki ake. Lembani mavesi ena amene amakutsimikizirani kuti Yehova amakuganizirani.
MABODZA OMWE SATANA AMANENA |
MMENE YEHOVA AMAONERA ATUMIKI AKE |
---|---|
Mulungu ali ndi mfundo zokhwima ndipo amaona kuti palibe chanzeru chimene atumiki ake angachite. Zolengedwa zake zonse sizingamusangalatse (Yobu 4:18; 25:5) |
Yehova amayamikira kwambiri tikamayesetsa kumutumikira modzichepetsa (Yobu 36:5) |
Munthu ndi wosafunika kwa Mulungu (Yobu 22:2) |
Yehova amasangalala ndiponso amatidalitsa tikamamutumikira mokhulupirika (Yobu 33:26; 36:11) |
Mulungu alibe nazo kanthu kuti ndiwe wolungama (Yobu 22:3) |
Yehova amasamalira olungama (Yobu 36:7) |