MOYO WATHU WACHIKHRISTU
Zofunika Kukumbukira Pamsonkhano Wachigawo
Pa nthawi ya msonkhano wachigawo tikufunitsitsa kudzasonyeza anthu chikondi ngati mmene timachitira nthawi zonse. (Mateyu 22:37-39) Lemba la 1 Akorinto 13:4-8, limafotokoza zimene chikondi chimachita, limati: “Chikondi n’choleza mtima ndiponso n’chokoma mtima. . . . sichichita zosayenera, sichisamala zofuna zake zokha, sichikwiya. . . . Chikondi sichitha.” Mukamaonera vidiyo ya Zofunika Kukumbukira Pamsonkhano Wachigawo, muziganizira mmene mungadzasonyezere ena chikondi pa nthawi ya msonkhano.
KODI TINGASONYEZE BWANJI CHIKONDI . . .
-
tikamasunga malo okhala?
-
nyimbo zomvetsera zikatsala pang’ono kuyamba?
-
kumalo ogona ngati tapeza malo kuhotelo kapenanso kwinakwake?
-
tikamadzipereka kugwira nawo ntchito zina?