April 4-10
YOBU 16-20
Nyimbo Na. 79 ndi Pemphero
Mawu Oyamba (Osapitirira 3 min.)
CHUMA CHOPEZEKA M’MAWU A MULUNGU
“Tizilimbikitsa Anzathu Powayankhula Mokoma Mtima”: (10 min.)
Yobu 16:4, 5—Munthu wopereka malangizo ayenera kuyankhula molimbikitsa kwa ena (w90 3/15 27 ndime 1-2)
Yobu 19:2—Yobu analira chifukwa cha mawu opweteka a Bilidadi (w06 3/15 15 ndime 5; w94 10/1 32)
Yobu 19:25—Chiyembekezo chakuti akufa adzauka chinathandiza Yobu pa nthawi yomwe anakumana ndi mayesero aakulu (w06 3/15 15 ndime 4; it-2-E 735 ndime 2-3)
Kufufuza Mfundo Zothandiza: (8 min.)
Yobu 19:20 [Mawu am’munsi]—Kodi Yobu ankatanthauza chiyani pamene ananena kuti, “Ndapulumuka ndi khungu la mano anga”? (w06 3/15 14 ndime 13; it-2-E 977 ndime 1)
Yobu 19:26—Popeza kuti munthu sangathe kuona Yehova, kodi Yobu ankatanthauza chiyani ponena kuti “ndidzaona Mulungu”? (w94 11/15 19 ndime 17)
Kodi ndaphunzira zotani zokhudza Yehova pa kuwerenga Baibulo kwa mlungu uno?
Kodi ndi mfundo ziti zimene ndaphunzira mlungu uno zimene ndingazigwiritse ntchito mu utumiki?
Kuwerenga Baibulo: Yobu 19:1-23 (Osapitirira 4 min.)
KUPHUNZITSA MWALUSO MU UTUMIKI
Kukonzekera Ulaliki wa Mwezi Uno: (15 min.) Nkhani yokambirana. Onetsani mavidiyo a zitsanzo za ulaliki ndipo kenako kambiranani mfundo zikuluzikulu za m’mavidiyowo. Limbikitsani ofalitsa kuti akonze ulaliki wawowawo.
MOYO WATHU WACHIKHRISTU
Nyimbo Na. 42
“Nkhani Zatsopano Zothandiza Poyamba Kukambirana ndi Anthu”: (10 min.) Nkhani yokambirana. Limbikitsani onse kuti azigwiritsa ntchito nkhani zakuti, “Kodi Baibulo Limanena Zotani?” pofuna kuyambitsa maphunziro a Baibulo.
Mafunso Ochokera kwa Owerenga: (5 min.) Nkhani yokambidwa ndi mkulu, kuchokera mu Nsanja ya Olonda ya February 15, 2015, tsamba 30, ndime 4-6.
Phunziro la Baibulo la Mpingo: cl mutu 28 ndime 10-17 (30 min.)
Mfundo Zimene Taphunzira Komanso za Mlungu Wamawa (3 min.)
Nyimbo Na. 65 ndi Pemphero