Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

Pitani ku mitu ya nkhani

CHUMA CHOPEZEKA M’MAWU A MULUNGU | YOBU 16-20

Tizilimbikitsa Anzathu Powayankhula Mokoma Mtima

Tizilimbikitsa Anzathu Powayankhula Mokoma Mtima

Munthu wopereka malangizo ayenera kuyankhula molimbikitsa kwa ena

16:4, 5

  • Yobu anavutika maganizo kwambiri, choncho ankafunika kulimbikitsidwa

  • Anzake atatu a Yobu sananene chilichonse chomulimbikitsa. Iwo ankangomuimba mlandu ndipo zinamusokoneza maganizo kwambiri

Yobu analira chifukwa cha mawu opweteka a Bilidadi

19:2, 25

  • Yobu anadandaulira Mulungu kuti amuthandize kupezako mpumulo, ngakhale kufa kumene

  • Yobu ankakhulupirira kwambiri kuti akufa adzauka ndipo anakhala wokhulupirika nthawi yonse yomwe anakumana ndi mavuto