Zitsanzo za Ulaliki
GALAMUKANI!
Perekani Magaziniyo: Ndikufuna ndikupatseni magazini yatsopano iyi ya Galamukani!
Funso: Taonani funso lomwe lili patsamba 2. Kodi inuyo mukuganiza bwanji?
Lemba: Luka 7:35
Nkhani imeneyi ikufotokoza mmene tingapindulire ndi mfundo za m’Baibulo.
GALAMUKANI!
Funso: Kodi nanunso mumaona kuti kutsatira mfundo ya palemba ili n’kothandiza?
Lemba: Mat. 6:34
Perekani Magaziniyo: [Tsegulani nkhani yakuti, “Zimene Baibulo Limanena—Nkhawa.”] Nkhaniyi ikufotokoza mmene Baibulo lingatithandizire tikakhala ndi nkhawa.
Baibulo Limaphunzitsa Chiyani
Funso: Anthu ambiri amene amakhulupirira Mulungu, amafunitsitsa kumudziwa bwino. Kodi mukudziwa kuti Baibulo limatilimbikitsa kuti tiyandikire Mulungu?
Lemba: Yak. 4:8a
Perekani Bukulo: Buku ili linalembedwa n’cholinga chotithandiza kuphunzira za Mulungu pogwiritsa ntchito Baibulo. [Sonyezani mutu woyamba wa buku la Baibulo Limaphunzitsa Chiyani.]
LEMBANI ULALIKI WANUWANU
Potengera zitsanzozi, konzani njira imene mungagwiritse ntchito.