Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

Pitani ku mitu ya nkhani

MOYO WATHU WACHIKHRISTU

Tidzagwira Ntchito Yapadera Yogawira Nsanja ya Olonda mu September

Tidzagwira Ntchito Yapadera Yogawira Nsanja ya Olonda mu September

Anthu padzikoli akukumana ndi mavuto ambiri ndipo akufunika kuthandizidwa. (Mlal. 4:1) M’mwezi wonse wa September chaka chino, tidzagwira ntchito yapadera yogawira magazini ya Nsanja ya Olonda. Magaziniyi ili ndi nkhani zomwe zingalimbikitse anthu pa mavuto amene akukumana nawo. Tiyeni tidzayesetse kugawira anthu ambiri magazini imeneyi. Popeza tikufuna kudzalankhula ndi anthu pamaso ndi pamaso kuti tiwalimbikitse, tisadzasiye magaziniwa pakhomo lomwe sitinapeze anthu.

ZIMENE TINGANENE

Munganene kuti, “Tonse timakumana ndi mavuto ndipo timafunika kulimbikitsidwa. Koma kodi ndi ndani amene angatithandize tikakhala pamavuto? [Werengeni 2 Akorinto 1:3, 4.] Magaziniyi ikufotokoza mmene Mulungu amatithandizira tikamakumana ndi mavuto.”

Ngati munthuyo akusonyeza kuti akufuna kudziwa zambiri, m’patseni magaziniyo ndipo kenako, . . .

MUONETSENI VIDIYO YAKUTI N’CHIFUKWA CHIYANI TIYENERA KUPHUNZIRA BAIBULO?

Kenako m’pempheni kuti muziphunzira naye Baibulo.

MUFUNSENI FUNSO LIMENE MUDZAKAMBIRANE PA ULENDO WOTSATIRA