Zitsanzo za Ulaliki
GALAMUKANI!
Funso: Kodi mukuganiza kuti zinthu zingakhale bwino padzikoli ngati anthu onse atasiya zoipa zimene anazolowera kuchita n’kumayesetsa kuchita zabwino?
Lemba: Mlal. 7:8a
Perekani Magaziniyo: Nkhani za m’magaziniyi zikufotokoza mfundo za m’Baibulo zomwe zingathandize anthu kuti azikonda kuchita zinthu zabwino.
GALAMUKANI!
Funso: Nthawi zina zinthu zingasinthe mosayembekezereka pa moyo wathu ndipo palibe zomwe tingachite kuti zimenezi zisachitike. Kodi mukuganiza kuti munthu angatani ngati zinthu zasintha pa moyo wake?
Lemba: Mlal. 7:10
Perekani magaziniyo: [Musonyezeni nkhani imene ikuyambira patsamba 10.] Nkhaniyi ikufotokoza mfundo za m’Baibulo zimene zingatithandize zinthu zikasintha pa moyo wathu.
MVERANI MULUNGU KUTI MUDZAPEZE MOYO WOSATHA
Funso: Aliyense, kuphatikizapo achibale komanso anzathu, ali ndi dzina. Koma nanga bwanji Mulungu, kodi nayenso ali ndi dzina? Nanga dzina lake ndi ndani?
Lemba: Sal. 83:18
Perekani Kabukuko: Kabuku aka kakufotokoza zinthu zinanso zomwe Baibulo limanena zokhudza Mulungu. [Musonyezeni tsamba 6 ndi 7.]
LEMBANI NJIRA INA IMENE MUNGAGWIRITSE NTCHITO
Potengera zitsanzozi, konzani njira imene mungagwiritse ntchito.