Anasankha Zochita Pogwiritsa Ntchito Mawu a Mulungu
Kodi tikuphunzira chiyani pa nkhani yokhudza mmene nkhani yamdulidwe inathetsedwera?
15:1, 2—Tizikhala odzichepetsa komanso oleza mtima. M’malo mothetsa nkhaniyi okha, Paulo ndi Baranaba anapempha malangizo kuchokera ku gulu la Yehova.
15:28, 29—Tizidalira gulu la Yehova. Mpingo unkakhulupirira kuti Yehova apitiriza kuutsogolera pogwiritsa ntchito mzimu woyera komanso Khristu Yesu.
16:4, 5—Tizikhala omvera. Mipingo inapitiriza kukulirakulira pamene inkatsatira malangizo ochokera ku bungwe lolamulira.