NDANDANDA YA UTUMIKI KOMANSO MOYO WATHU WACHIKHRISTU February 2018
Zimene Tinganene
Kukambirana pogwiritsa ntchito mafunso otsatirawa: Kodi inuyo mumaona kuti Baibulo ndi lothandizabe masiku ano? Kodi zimene Baibulo limanena zimagwirizana ndi sayansi? Kodi malangizo a m’Baibulo ndi othandizadi?
CHUMA CHOPEZEKA M’MAWU A MULUNGU
Fanizo la Tirigu ndi Namsongole
Kodi Yesu anagwiritsa ntchito fanizo la tirigu ndi namsongole pofuna kunena za chiyani? Kodi ndi ndani yemwe ali wofesa mbewu, mdani, komanso okolola?
MOYO WATHU WACHIKHRISTU
Mfundo Zimene Tingaphunzire Kuchokera M’mafanizo Onena za Ufumu
Yesu ankagwiritsa ntchito mafanizo osavuta kumva pophunzitsa mfundo zozama zachoonadi. Kodi tingaphunzire chiyani pa Mateyu 13?
CHUMA CHOPEZEKA M’MAWU A MULUNGU
Yesu Amadyetsa Anthu Ambiri Kudzera Mwa Anthu Ochepa
Yesu anauza ophunzira ake kuti adyetse khamu la anthu ngakhale kuti anali ndi mikate 5 komanso nsomba ziwiri zokha. Kodi chinachitika n’chiyani, nanga zimenezi zinkatanthauza chiyani?
MOYO WATHU WACHIKHRISTU
“Uzilemekeza Bambo Ako ndi Mayi Ako”
Pamene Yesu anali padzikoli, anauza anthu lamulo lakuti: “Uzilemekeza bambo ako ndi mayi ako.” Kodi tiyenera kumvera lamuloli ngakhale makolo athu atakalamba?
CHUMA CHOPEZEKA M’MAWU A MULUNGU
Kodi Mumayendera Maganizo a Ndani?
Kodi tiyenera kuchita chiyani kuti tizitsogoleredwa ndi Mulungu osati Satana? Yesu anatchula zinthu zitatu zomwe zingatithandize kuti tisamakhale ndi maganizo olakwika.
MOYO WATHU WACHIKHRISTU
Kuwonjezera Luso Lathu Mu Utumiki—Muzigwiritsa Ntchito Mafunso Mwaluso
Yesu ankakonda kufunsa mafunso amene ankachititsa ophunzira ake kufotokoza maganizo awo. Kodi tingatengere bwanji chitsanzo chake tikamalalikira komanso kuphunzitsa anthu?
CHUMA CHOPEZEKA M’MAWU A MULUNGU
Tizipewa Kuchita Zinthu Zimene Zingakhumudwitse Ena
Yesu anagwiritsa ntchito mafanizo pophunzitsa anthu za kuopsa kochita zinthu zimene zingatipunthwitse komanso kukhumudwitsa ena. Kodi n’chiyani pa moyo wanu chimene chingakhale chopunthwitsa?