February 12-18
MATEYU 14-15
Nyimbo Na. 93 ndi Pemphero
Mawu Oyamba (Osapitirira 3 min.)
CHUMA CHOPEZEKA M’MAWU A MULUNGU
“Yesu Amadyetsa Anthu Ambiri Kudzera Mwa Anthu Ochepa”: (10 min.)
Mat. 14:16, 17—Ophunzira a Yesu anali ndi mitanda 5 ya mkate ndi nsomba ziwiri (w13 7/15 15 ¶2)
Mat. 14:18, 19—Yesu anadyetsa khamu lalikulu la anthu pogwiritsa ntchito ophunzira ake (w13 7/15 15 ¶3)
Mat. 14:20, 21—Anthu ambirimbiri anapindula ndi chozizwitsa chimene Yesu anachita (“osawerengera akazi ndi ana aang’ono” mfundo zimene ndikuphunzira pa Mat. 14:21, nwtsty; w13 7/15 15 ¶1)
Kufufuza Mfundo Zothandiza: (8 min.)
Mat. 15:7-9—N’chifukwa chiyani tiyenera kupewa chinyengo? (“Onyenga” mfundo zimene ndikuphunzira pa Mat. 15:7, nwtsty)
Mat. 15:26—Kodi n’kutheka kuti Yesu ankatanthauza chiyani pamene ananena mawu akuti “tiagalu”? (“ana . . . tiagalu” mfundo zimene ndikuphunzira pa Mat. 15:26, nwtsty)
Kodi mwaphunzira zotani zokhudza Yehova pa kuwerenga Baibulo kwa mlungu uno?
Kodi ndi mfundo zina ziti zothandiza zimene mwapeza pa kuwerenga Baibulo kwa mlungu uno?
Kuwerenga Baibulo: (Osapitirira 4 min.) Mat. 15:1-20
KUPHUNZITSA MWALUSO MU UTUMIKI
Ulendo Woyamba: (Osapitirira 2 min.) Gwiritsani ntchito chitsanzo cha zimene tinganene.
Vidiyo ya Ulendo Wobwereza Woyamba: (5 min.) Onerani ndi kukambirana mfundo za m’vidiyoyi.
Nkhani: (Osapitirira 6 min.) w15 9/15 16-17 ¶14-17—Mutu: Tizitsatira Yesu Kuti Tilimbitse Chikhulupiriro Chathu.
MOYO WATHU WACHIKHRISTU
Khalani Bwenzi la Yehova—Mmene Mungapezere Anzanu: (7 min.) Onetsani vidiyoyi. Kenako pemphani ana amene munawasankhiratu kuti abwere kupulatifomu ndipo muwafunse mafunso otsatirawa: N’chifukwa chiyani muyenera kukhala ndi anzanu amene amakonda Yehova? Kodi mungaphunzire chiyani kwa anzanu oterowo?
“Uzilemekeza Bambo Ako ndi Mayi Ako”: (8 min.) Nkhani yokambirana. Onetsani vidiyo yakuti Kodi Ndingatani Kuti Ndizilankhulana Bwino ndi Makolo Anga?
Phunziro la Baibulo la Mpingo: (30 min.) kr mutu 14 ¶1-7
Mfundo Zimene Taphunzira Komanso za Mlungu Wamawa (3 min.)
Nyimbo Na. 148 ndi Pemphero