MOYO WATHU WACHIKHRISTU
Mfundo Zimene Tingaphunzire Kuchokera M’mafanizo Onena za Ufumu
Yesu ankagwiritsa ntchito mafanizo osavuta kumva pophunzitsa mfundo zozama zachoonadi. Komabe, ndi anthu odzichepetsa okha amene ankamvetsa komanso kugwiritsa ntchito mfundo zomwe ankaphunzira m’mafanizowa. (Mat. 13:10-15) Pa mafanizo onena za Ufumu otsatirawa, yankhani mafunso awa: Kodi ndikuphunzira chiyani m’fanizoli? Kodi zimene ndikuphunzirazi ndingazigwiritse ntchito bwanji pa moyo wanga?
UFUMU WAKUMWAMBA ULI NGATI . . .
-
“kanjere ka mpiru.”—Mat. 13:31, 32; w14 12/15 8 ¶9.
-
“zofufumitsa.”—Mat. 13:33; w14 12/15 9-10 ¶14-15.
-
“chuma” ndi “wamalonda woyendayenda.”—Mat. 13:44-46; w14 12/15 10 ¶18.