Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

Pitani ku mitu ya nkhani

MOYO WATHU WACHIKHRISTU

Muzipindula Mokwanira Mukamaphunzira Panokha

Muzipindula Mokwanira Mukamaphunzira Panokha

KODI ZIMENEZI N’ZOFUNIKA BWANJI? Tikamaphunzira Mawu a Mulungu patokha, timadziwa bwino “m’lifupi ndi m’litali ndi kukwera ndi kuzama” kwa choonadi. (Aef. 3:18) Kuphunzira patokha kumatithandiza kuti tikhale osalakwa komanso opanda chilema m’dziko loipali. Kumatithandizanso kuti tipitirize “kugwira mwamphamvu mawu amoyo.” (Afil. 2:15, 16) Tikamaphunzira Mawu a Mulungu timatha kusankha zomwe tikufuna kuphunzira malinga ndi zimene tikufunikira. Kodi tingatani kuti tizipindula kwambiri tikamawerenga komanso kuphunzira Baibulo?

KODI TINGACHITE BWANJI ZIMENEZI?

  • Muzilemba mzere kunsi kwa mavesi komanso notsi m’Baibulo lanu

  • Mukamawerenga Mawu a Mulungu muzidzifunsa mafunso monga akuti: ‘Nkhaniyi ikunena za ndani? Chinachitika n’chiyani? Zinachitikira kuti? Zinachitika bwanji? N’chifukwa chiyani zinachitika choncho?’

  • Muzifufuza. Mungagwiritse ntchito zipangizo zofufuzira zimene muli nazo ndipo mukhoza kufufuza pogwiritsa ntchito mitu ya nkhani kapena mavesi a m’Baibulo

  • Muziganizira mozama zimene mwawerengazo n’kuona mmene zikukukhudzirani

  • Muzigwiritsa ntchito zimene mwaphunzira.​—Luka 6:47, 48

ONERANI VIDIYO YAKUTI PITIRIZANI “KUGWIRA MWAMPHAMVU MAWU AMOYO” POPHUNZIRA MWAKHAMA, KENAKO YANKHANI MAFUNSO OTSATIRAWA:

  • Kodi ena apindula bwanji chifukwa chophunzira pawokha?

  • N’chifukwa chiyani tiyenera kupemphera tisanayambe kuphunzira patokha?

  • Kodi n’chiyani chingatithandize kuti tizimvetsa bwino zimene tikuwerenga m’Baibulo?

  • Kodi ndi zizindikiro ziti zomwe tingalembe m’Baibulo lathu tikamaphunzira patokha?

  • Kodi kuganizira zomwe tikuwerenga n’kofunika bwanji?

  • N’chifukwa chiyani tiyenera kugwiritsa ntchito zimene taphunzira?

“Ndimakonda kwambiri chilamulo chanu! Ndimasinkhasinkha chilamulocho tsiku lonse.”​—Sal. 119:97