Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

Pitani ku mitu ya nkhani

MOYO WATHU WACHIKHRISTU

Muzithandiza Banja Lanu Kuti Lizikumbukira Yehova

Muzithandiza Banja Lanu Kuti Lizikumbukira Yehova

Yeremiya anapatsidwa ntchito yochenjeza Ayuda kuti adzawonongedwa chifukwa chakuti anaiwala Mulungu wawo Yehova. (Yer. 13:25) Kodi n’chiyani chinachititsa kuti zinthu zifike poipa chonchi ku Yuda? Mabanja achiisiraeli anali atasiya kukonda Yehova. Zikuoneka kuti amuna amene anali ndi banja sankatsatira malangizo amene Yehova anapereka pa Deuteronomo 6:5-7.

Masiku ano mabanja amene amakonda kwambiri Yehova amathandiza kuti zinthu ziziyenda bwino mumpingo. Amuna angathandize anthu a m’banja lawo kuti azikumbukira Yehova pochita nawo Kulambira kwa Pabanja nthawi zonse komanso m’njira yabwino. (Sal. 22:27) Pambuyo poonetsa vidiyo yakuti Mawu Awa . . . Azikhala Pamtima Pako”Kucheza ndi Mabanja, kambiranani mafunso awa:

  • Kodi mabanja ena athana bwanji ndi mavuto amene ambiri amakumana nawo pochita Kulambira kwa Pabanja?

  • Kodi timapindula bwanji tikamachita Kulambira kwa Pabanja nthawi zonse komanso m’njira yabwino?

  • Kodi ndi mavuto ati amene mumakumana nawo okhudza Kulambira kwa Pabanja, nanga mungawathetse bwanji?