March 19-25
Mateyu 24
Nyimbo Na. 126 ndi Pemphero
Mawu Oyamba (Osapitirira 3 min.)
CHUMA CHOPEZEKA M’MAWU A MULUNGU
“Pitirizani Kukhala Maso M’masiku Otsiriza Ano” (10 min.)
Mat. 24:12—Kuwonjezeka kwa kusamvera malamulo kwachititsa kuti chikondi cha anthu ambiri chizirale (it-2 279 ¶6)
Mat. 24:39—Anthu ena akutanganidwa ndi zinthu zatsiku ndi tsiku ndipo zawachititsa kuti azilephera kutumikira Mulungu bwinobwino (w99 11/15 19 ¶5)
Mat. 24:44—Ambuye adzabwera pa nthawi imene anthu sakuyembekezera (jy 259 ¶4)
Kufufuza Mfundo Zothandiza: (8 min.)
Mat. 24:8—Kodi n’kutheka kuti mawu a Yesuwa akutanthauza chiyani? (Mfundo zimene ndikuphunzira za “chiyambi cha masautso” pa Mat. 24:8, nwtsty)
Mat. 24:20—N’chifukwa chiyani Yesu analankhula mawu amenewa? (Mfundo zimene ndikuphunzira za “m’nyengo ya chisanu,” “pa tsiku la sabata” pa Mat. 24:20, nwtsty)
Kodi mwaphunzira zotani zokhudza Yehova pa kuwerenga Baibulo kwa mlungu uno?
Kodi ndi mfundo zina ziti zothandiza zimene mwapeza pa kuwerenga Baibulo kwa mlungu uno?
Kuwerenga Baibulo: (Osapitirira 4 min.) Mat. 24:1-22
KUPHUNZITSA MWALUSO MU UTUMIKI
Ulendo Woyamba: (Osapitirira 2 min.) Yambani ndi chitsanzo cha ulendo woyamba. Sonyezani mmene mungayankhire pa nkhani inayake yomwe anthu a m’gawo lanu amatsutsa kawirikawiri.
Ulendo Wobwereza Woyamba: (Osapitirira 3 min.) Yambani ndi chitsanzo cha ulendo wobwereza woyamba. Munthu amene munacheza naye ulendo wapita simunamupeze pakhomo koma mwapeza wachibale wake.
Vidiyo ya Ulendo Wobwereza Wachiwiri: (5 min.) Onerani ndi kukambirana mfundo za m’vidiyoyi.
MOYO WATHU WACHIKHRISTU
“Mapeto a Dziko Loipali Ali Pafupi Kwambiri”: (15 min.) Nkhani yokambirana. Onetsani vidiyoyi.
Phunziro la Baibulo la Mpingo: (30 min.) kr mutu 15 ¶18-28
Mfundo Zimene Taphunzira Komanso za Mlungu Wamawa (3 min.)
Nyimbo Na. 97 ndi Pemphero