CHUMA CHOPEZEKA M’MAWU A MULUNGU
Samalani Kuti Musakhale Wonyada Ndi Wodzidalira
Kora anagalukira dongosolo la Yehova chifukwa anayamba kunyada ndi kudzidalira (Nu 16:1-3; w11 9/15 27 ¶12)
Kora anali Mlevi wolemekezeka ndipo anali kale ndi maudindo ambiri (Nu 16:8-10; w11 9/15 27 ¶11)
Maganizo olakwika a Kora anabweretsa mavuto aakulu (Nu 16:32, 35)
Tisalole kuti zimene takwanitsa kuchita m’gulu la Yehova zitichititse kuyamba kunyada komanso kudzidalira. Ngati takhala m’choonadi kwa nthawi yaitali komanso ngati tili ndi maudindo akuluakulu, m’pamene tiyeneranso kukhala odzichepetsa kwambiri.