MOYO WATHU WACHIKHRISTU
Muzisankha Zinthu Mwanzeru pa Nkhani ya Mowa
Akhristu onse ayenera kuchita zinthu modziletsa pa nkhani ya mowa. (Miy 23:20, 29-35; 1Ak 6:9, 10) Ngati Mkhristu wasankha kumwa mowa, sayenera kumwa kwambiri. Akuyeneranso kupeweratu kudalira mowa kuti achite zinazake komanso sakuyenera kukhumudwitsa anthu ena. (1Ak 10:23, 24; 1Ti 5:23) Sitikuyenera kukakamiza aliyense kuti amwe mowa, makamaka ana.
ONERANI VIDIYO YAMAKATUNI YAKUTI GANIZIRANI ZIMENE ZINGACHITIKE NGATI MUTAMWA MOWA, NDIPO KENAKO YANKHANI MAFUNSO OTSATIRAWA:
-
N’chifukwa chiyani Akhristu onse ayenera kutsatira malamulo a m’dera lawo pa nkhani yomwa mowa?—Aro 13:1-4
-
N’chifukwa chiyani sitiyenera kulola anthu ena kutikakamiza kuti timwe mowa?—Aro 6:16
-
Kodi tingapewe bwanji mavuto omwe angabwere chifukwa cha mowa?