MOYO WATHU WACHIKHRISTU
“Chikondi . . . Sichidzikuza”
Chikondi chimatithandiza kuti tizisonyeza kuti ndife odzichepetsa. (1Ak 13:4) Tikamakonda abale athu, sitimadziona kukhala ofunika kwambiri kuposa iwowo. Timaona zabwino mwa anthu ena ndipo timagwiritsa ntchito maluso athu powathandiza. (Afi 2:3, 4) Tikamakonda kwambiri abale athu, ndi pamene Yehova angamatigwiritse ntchito pochita chifuniro chake.
ONERANI VIDIYO YAKUTI MUZIKUMBUKIRA ZIMENE CHIKONDI CHIMACHITA KOMANSO ZIMENE SICHICHITA—SICHIDZIKUZA, KENAKO YANKHANI MAFUNSO OTSATIRAWA:
-
Kodi Abisalomu anali ndi mphatso ziti?
-
Kodi anagwiritsa ntchito bwanji molakwika mphatso zakezi?
-
Kodi tingatani kuti tipewe kudzikuza?—Aga 5:26