June 6-12
2 SAMUELI 9-10
Nyimbo Na. 124 ndi Pemphero
Mawu Oyamba (1 min.)
CHUMA CHOPEZEKA M’MAWU A MULUNGU
“Davide Anasonyeza Chikondi Chokhulupirika”: (10 min.)
Mfundo Zothandiza: (10 min.)
2Sa 10:4, 5—N’chifukwa chiyani zimene Hanuni anachita zinali zochititsa manyazi amuna a Chiisiraeli? (it-1 266)
Pa kuwerenga Baibulo kwa mlungu uno, kodi mwapeza mfundo ziti zokhudza Yehova, utumiki kapena zinthu zina?
Kuwerenga Baibulo: (4 min.) 2Sa 9:1-13 (th phunziro 12)
KUPHUNZITSA MWALUSO MU UTUMIKI
Ulendo Woyamba: (3 min.) Gwiritsani ntchito chitsanzo cha ulendo woyamba. Sonyezani mmene mungayankhire munthu amene wanena zinthu zomwe anthu amakonda kunena ngati sakufuna kuti tikambirane nawo. (th phunziro 3)
Ulendo Wobwereza: (4 min.) Yambani ndi chitsanzo cha ulendo wobwereza. Kenako mugawireni kabuku kakuti Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale, ndipo kambiranani mwachidule zimene zili pa gawo lakuti “Zimene Mungachite Kuti Muzipindula Ndi Phunziro Lililonse.” (th phunziro 17)
Phunziro la Baibulo: (5 min.) lff phunziro 05 mfundo 4 (th phunziro 13)
MOYO WATHU WACHIKHRISTU
Muzikumbukira Zimene Chikondi Chimachita Komanso Zimene Sichichita—N’chokoma Mtima: (5 min.) Nkhani yokambirana. Onerani vidiyoyi. Kenako funsani mafunso otsatirawa: Kodi Davide anamusonyeza bwanji kukoma mtima Mefiboseti? Kodi tingasonyeze bwanji kukoma mtima komanso chikondi chokhulupirika kwa anthu ena?
Zimene Gulu Lathu Lachita: (10 min.) Onerani vidiyo ya Zimene Gulu Lathu Lachita ya June.
Phunziro la Baibulo la Mpingo: (30 min.) lff phunziro 07
Mawu Omaliza (3 min.)
Nyimbo Na. 1 ndi Pemphero