MOYO WATHU WACHIKHRISTU
“Chikondi . . . Sichikondwera ndi Zosalungama”
Zinthu zonse zimene Akhristu oona amachita, zimatsogoleredwa ndi chikondi. Chikondi “Sichikondwera ndi zosalungama.” (1Ak 13:4, 6) Choncho tiyenera kupeweratu zosangalatsa zimene zimalimbikitsa zachiwerewere komanso zachiwawa. Ndiponso sitimasangalala anthu ena akamakumana ndi zinthu zoipa, ngakhale amene anatilakwira.—Miy 17:5.
ONERANI VIDIYO YAKUTI MUZIKUMBUKIRA ZIMENE CHIKONDI CHIMACHITA KOMANSO ZIMENE SICHICHITA—SICHIKONDWERA NDI ZOSALUNGAMA, KENAKO YANKHANI MAFUNSO OTSATIRAWA:
-
Kodi Davide anatani atauzidwa kuti Yonatani ndi Sauli aphedwa?
-
Kodi ndi nyimbo yoimba polira iti imene Davide anapekera Sauli ndi Yonatani?
-
N’chifukwa chiyani Davide sanasangalale atamva kuti Sauli wamwalira?