Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

Pitani ku mitu ya nkhani

MOYO WATHU WACHIKHRISTU

Kodi Mwakonzeka Kukumana ndi Mavuto Azachuma?

Kodi Mwakonzeka Kukumana ndi Mavuto Azachuma?

Sitimadabwa kuona zochitika za padzikoli zikuchititsa kuti pakhale mavuto azachuma padziko lonse. N’chifukwa chiyani? Chifukwa tikukhala kumapeto kwenikweni kwa masiku otsiriza, ndipo Baibulo linatichenjezeratu kuti tisamadalire “chuma chosadalirika.” (1Ti 6:17; 2Ti 3:1) Kodi tingaphunzire chiyani kwa Mfumu Yehosafati pa nkhani ya kukonzekera kukumana ndi mavuto azachuma?

Ataopsezedwa ndi mitundu yodana nawo, Yehosafati anadalira Yehova. (2Mb 20:9-12) Mwamsanga, iye anachitanso zonse zofunika pokonzekera. Anamanga mizinda yokhala ndi mipanda yolimba, komanso anamanga mizinda ya asilikali. (2Mb 17:1, 2, 12, 13) Mofanana ndi Yehosafati, timafunika kulimbitsa ubwenzi wathu ndi Yehova ndipo tizichita zonse zomwe tingathe pokonzekera kukumana ndi mavuto.

ONERANI VIDIYO YAKUTI KODI MWAKONZEKA KUKUMANA NDI NGOZI ZOGWA MWADZIDZIDZI?, KENAKO YANKHANI MAFUNSO OTSATIRAWA:

  • Kodi tingakonzekere bwanji ngozi zadzidzidzi?

  • Kodi tingakonzekere bwanji kuthandiza ena?