Pamsonkhano wachigawo ku Malawi, anthu asonkhana madzulo kuti aonere JW Broadcasting

NDANDANDA YA UTUMIKI KOMANSO MOYO WATHU WACHIKHRISTU November 2019

Zimene Tinganene

Zitsanzo za zimene tinganene zofotokoza cholinga chimene Mulungu analengera anthu komanso zomwe walonjeza m’tsogolomu.

CHUMA CHOPEZEKA M’MAWU A MULUNGU

Musamakonde Dziko Kapena Zinthu za M’dziko

N’chiyani chimene tingachite kuti zinthu zam’dzikoli zisatilepheretse kutumikira Yehova?

MOYO WATHU WACHIKHRISTU

Musamatengere Maganizo a M’dzikoli Mukamakonzekera Ukwati

Kodi ndi mfundo za m’Baibulo ziti zomwe zingathandize anthu amene akufuna kukwatirana kukonzekera bwino tsiku la ukwati wawo kuti asadzadziimbe mlandu kapena kunong’oneza bondo?

CHUMA CHOPEZEKA M’MAWU A MULUNGU

Tiyenera Kuchita Khama Kuti Tikhalebe m’Choonadi

Kodi tingatani kuti ‘tizimenya mwamphamvu nkhondo yachikhulupiriro’?

CHUMA CHOPEZEKA M’MAWU A MULUNGU

“Ndikudziwa Ntchito Zako”

Yesu amadziwa chilichonse chomwe chikuchitika mumpingo ndipo ndi amene amatsogolera mabungwe a akulu.

MOYO WATHU WACHIKHRISTU

Yehova Amadziwa Zimene Timafunikira

N’chifukwa chiyani msonkhano wachigawo uliwonse umakhala wapanthawi yake? N’chiyani chimachititsa kuti misonkhano ya mkati mwa mlungu izikhala yolimbikitsa komanso yothandiza?

CHUMA CHOPEZEKA M’MAWU A MULUNGU

Anthu 4 Okwera Pamahatchi

Masiku ano tikuona zotsatira za anthu 4 okwera pamahatchi otchulidwa m’buku la Chivumbulutso. Kodi okwera pamahatchi amenewa akuimira chiyani?

MOYO WATHU WACHIKHRISTU

Yehova Amakonda Munthu Wopereka Mokondwera

Kodi mungapereke bwanji ndalama zothandizira ntchito yomwe a Mboni za Yehova amagwira padziko lonse?