Yesu Anachitira Umboni Choonadi
Yesu anachitira umboni choonadi chokhudza zolinga za Mulungu
-
M’MAWU: Iye ankalalikira mwakhama choonadi chonena za Ufumu wa Mulungu
-
M’ZOCHITA: Zimene anachita pa moyo wake zinasonyeza kuti maulosi a m’Baibulo ndi olondola
Nafenso monga otsatira a Yesu, timachitira umboni choonadi
-
M’MAWU: Ngakhale ena azitinyoza, timalalikira mwakhama uthenga wabwino wonena za Ufumu wa Mulungu womwe Mfumu yake ndi Yesu Khristu
-
M’ZOCHITA: Timasonyeza kuti tili ku mbali ya ulamuliro wa Yesu tikamachita zimene Mulungu amafuna komanso tikamapewa kukhala mbali ya dziko