October 8-14
YOHANE 11-12
Nyimbo Na. 16 ndi Pemphero
Mawu Oyamba (Osapitirira 3 min.)
CHUMA CHOPEZEKA M’MAWU A MULUNGU
“Muzitsanzira Yesu pa Nkhani Yochitira Ena Chifundo”: (10 min.)
Yoh. 11:23-26—Yesu analimbikitsa Marita (“Ndikudziwa kuti adzauka” mfundo zimene ndikuphunzira pa Yoh. 11:24, nwtsty; “Ine ndine kuuka ndi moyo” mfundo zimene ndikuphunzira pa Yoh. 11:25, nwtsty)
Yoh. 11:33-35—Yesu anamva chisoni kwambiri ataona Mariya komanso anthu ena akulira (“kulira,” “anadzuma . . . ndi kumva chisoni,” “povutika mumtima” mfundo zimene ndikuphunzira pa Yoh. 11:33, nwtsty; “anagwetsa misozi” mfundo zimene ndikuphunzira pa Yoh. 11:35, nwtsty)
Yoh. 11:43, 44—Yesu anawachitira chifundo n’kuwathandiza
Kufufuza Mfundo Zothandiza: (8 min.)
Yoh. 11:49—Kodi ndi ndani amene anasankha Kayafa kuti akhale mkulu wa ansembe, nanga anakhala paudindowu kwa nthawi yaitali bwanji? (“mkulu wa ansembe” mfundo zimene ndikuphunzira pa Yoh. 11:49, nwtsty)
Yoh. 12:42—N’chifukwa chiyani Ayuda ena ankachita mantha kuvomereza kuti Yesu ndi Khristu? (“olamulira,” “angawachotse musunagoge” mfundo zimene ndikuphunzira pa Yoh. 12:42, nwtsty)
Kodi mwaphunzira zotani zokhudza Yehova pa kuwerenga Baibulo kwa mlungu uno?
Kodi ndi mfundo zina ziti zothandiza zimene mwapeza pa kuwerenga Baibulo kwa mlungu uno?
Kuwerenga Baibulo: (Osapitirira 4 min.) Yoh. 12:35-50
KUPHUNZITSA MWALUSO MU UTUMIKI
Ulendo Woyamba: (Osapitirira 2 min.) Gwiritsirani ntchito chitsanzo cha ulendo woyamba.
Vidiyo ya Ulendo Wobwereza Woyamba: (5 min.) Onerani ndi kukambirana mfundo za m’vidiyoyi.
Nkhani: (Osapitirira 6 min.) w13 9/15 32—Mutu: N’chifukwa Chiyani Yesu Analira Asanaukitse Lazaro?
MOYO WATHU WACHIKHRISTU
Yesu Ndi “Kuuka ndi Moyo” (Yoh. 11:25): (15 min.) Nkhani yokambirana. Onetsani mbali ina ya vidiyo yakuti, “Mulungu Anamuika Kukhala Ambuye ndi Khristu”—Mbali Yachiwiri. Kenako funsani omvera mafunso otsatirawa: Kodi nkhani imeneyi ikutithandiza bwanji kudziwa kuti Yesu anali wachifundo kwambiri? Kodi Yesu ndi “kuuka ndi moyo” m’njira yotani? Kodi Yesu adzachita zozizwitsa zotani m’tsogolo?
Phunziro la Baibulo la Mpingo: (30 min.) jy mutu 8
Mfundo Zimene Taphunzira Komanso za Mlungu Wamawa (3 min.)
Nyimbo Na. 148 ndi Pemphero