Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

Pitani ku mitu ya nkhani

Zitsanzo za Ulaliki

Zitsanzo za Ulaliki

NSANJA YA OLONDA

Funso: Tonsefe timafunika kuthandizidwa tikakumana ndi mavuto. Koma kodi ndi ndani angatithandize tikakhala pamavuto?

Lemba: 2 Akor. 1:3, 4

Perekani Magaziniyo: Maganiziyi ikufotokoza zimene Mulungu amachita kuti atithandize tikakumana ndi mavuto.

NSANJA YA OLONDA (tsamba lomaliza)

Funso: Anthu ena amaganiza kuti Ufumu wa Mulungu uli mumtima mwa munthu, pomwe ena amaganiza kuti Ufumu wa Mulungu udzakhalapo anthu akadzakwanitsa kukhazikitsa mtendere ndiponso mgwirizano padzikoli. Inuyo mukuganiza bwanji?

Lemba: Dan. 2:44

Perekani Magaziniyo: Lembali likusonyeza kuti Ufumu wa Mulungu ndi boma lenileni. Nkhaniyi ikufotokozanso zinthu zina zimene Baibulo limanena zokhudza Ufumu wa Mulungu

KUPHUNZITSA CHOONADI

Funso: Kodi tingadziwe bwanji kuti Mulungu amatiganizira?

Lemba: 1 Pet. 5:7

Zoona Zake: Yehova amatiganizira, n’chifukwa chake amatiuza kuti tizipemphera kwa iye.

LEMBANI ULALIKI WANUWANU

Potengera zitsanzozi, konzani njira imene mungagwiritse ntchito.