Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

Pitani ku mitu ya nkhani

Ziwerengero Zonse za 2022

Ziwerengero Zonse za 2022
  • Nthambi za Mboni za Yehova:  86

  • Mayiko Amene Anatumiza Lipoti: 239

  • Mipingo Yonse: 117,960

  • Opezeka pa Chikumbutso Padziko Lonse: 19,721,672

  • Amene Anadya Zizindikiro Padziko Lonse: 21,150

  • Ofalitsa Onse Amene Anagwira Ntchito Yolalikira a: 8,699,048

  • Avereji ya Ofalitsa Amene Ankalalikira Mwezi Uliwonse: 8,514,983

  • Kuwonjezereka kwa Ofalitsa Kuchokera mu 2021: 0.4

  • Obatizidwa Onse b: 145,552

  • Avereji ya Apainiya c Okhazikika Mwezi Uliwonse: 1,465,202

  • Avereji ya Apainiya Othandiza Mwezi Uliwonse: 381,310

  • Maola Onse Amene Tinalalikira: 1,501,797,703

  • Avereji ya Maphunziro a Baibulo d Mwezi Uliwonse: 5,666,996

M’chaka chautumiki cha 2022, e a Mboni za Yehova anagwiritsa ntchito ndalama zokwana madola 242 miliyoni posamalira apainiya apadera, amishonale ndi oyang’anira dera, pa utumiki wawo. Padziko lonse pali abale ndi alongo okwana 21,629 amene akutumikira m’maofesi a nthambi. Onsewa ali m’Gulu Lapadziko Lonse la Atumiki Apadera a Nthawi Zonse a Mboni za Yehova.

a Wofalitsa ndi munthu amene amalalikira mwakhama uthenga wabwino wa Ufumu wa Mulungu. (Mateyu 24:14) Kuti mudziwe mmene timapezera chiwerengerochi, onani nkhani ya pa jw.org yakuti “Kodi a Mboni za Yehova Alipo Angati Padziko Lonse?

b Kuti mudziwe zimene mungachite kuti mubatizidwe n’kukhala wa Mboni za Yehova, onani nkhani ya pa jw.org yakuti “Kodi Ndingatani Kuti Ndikhale wa Mboni za Yehova?

c Mpainiya ndi wa Mboni wobatizidwa komanso wachitsanzo chabwino amene amadzipereka kuti azilalikira uthenga wabwino kwa maola enaake mwezi uliwonse.

d Kuti mudziwe zambiri, onani nkhani ya pa jw.org yakuti “Kodi Phunziro la Baibulo Lomwe a Mboni za Yehova Amachititsa Limakhala Lotani?

e Chaka chautumiki cha 2022 chinayamba pa 1 September 2021, ndipo chinatha pa 31 August 2022.