Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

Pitani ku mitu ya nkhani

Phunziro 3

Phunziro 3

Davide wamva zoti mnzake akudwala.

Choncho akunena kuti: “Ndadziwa chochita.

Ndimulembera kalata yomulimbikitsa, ndipo kenako ndikam’patsa.”

Uzisonyeza ena chifundo, ndipo nonse mudzakhala osangalala.

ZOTI MUCHITE

Mwana wanuyo muwerengereni:

1 Petulo 3:8

Muuzeni mwanayo kuti aloze:

Nyumba Tebulo Davide

Dzuwa Mbalame Mtengo

Mufunseni mwana wanu kuti:

Kodi ukudziwa aliyense amene akudwala?

Kodi tingamuthandize bwanji kuti achire?