Pitani ku nkhani yake

Pitani ku mitu ya nkhani

Zimene Zachitika M’chaka Chapitachi

Zimene Zachitika M’chaka Chapitachi

Yehova Mulungu anauzira mneneri Yesaya kulosera kuti: “M’malo mwa mkuwa, ndidzabweretsa golide. M’malo mwa chitsulo, ndidzabweretsa siliva. M’malo mwa mtengo, ndidzabweretsa mkuwa ndipo m’malo mwa miyala, ndidzabweretsa chitsulo.” (Yes. 60:17) Lembali likusonyeza kuti zinthu wamba zikulowedwa m’malo ndi zinthu zamtengo wapatali. Izi zikuimira kupita patsogolo kwa gulu la Yehova. M’chaka chapitachi ulosiwu wakwaniritsidwa m’njira zambiri. Kunena zoona zinthu zakhala zikutiyendera bwino kwambiri m’nthawi yamapeto ino.—Mat. 24:3.

M'CHIGAWO ICHI

Zinthu Zikuyenda ku Warwick

Onani zinthu zosangalatsa zimene zachitika pamalo amene akumanga likulu la Mboni za Yehova.

Dipatimenti Yoona za Mapulani ndi Zomangamanga Padziko Lonse

Dipatimenti yatsopanoyi iyenera kuonetsetsa kuti ntchito yomanga ikuyenda bwinobwino kumalo oposa 13,000.

Baibulo la Dziko Latsopano Ndi Lolimba Kwambiri

Baibulo la Dziko Latsopano lokonzedwanso limene linatuluka mu 2013 ndi lokongola komanso lolimba kwambiri.

Msonkhano Waukulu Kwambiri wa Mboni za Yehova

Anthu ambirimbiri kuposa kale anamvetsera msonkhano wapachaka wa Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania wa nambala 129.

Mwambo Wotsegulira Ofesi ya Nthambi ku Sri Lanka

Anthu m’madera osiyanasiyana anatha kuonera pulogalamuyi m’masikirini.

Lipoti la Milandu

A Mboni za Yehova akuyesetsa kuti akhale ndi ufulu wolambira.

Malipoti Apadera a Zochitika M’mayiko Osiyanasiyana

N’chifukwa chiyani tiatsikana tina tiwiri tinapereka ndalama zogulira foni kuti zithandize pa ntchito yomanga Nyumba ya Ufumu?

“Taona Zodabwitsa”

Kodi ndi zinthu ziti masiku ano zimene zikufanana ndi zodabwitsa zimene zinkachitika Yesu ali padzikoli?