BOKOSI 13A
Akachisi Osiyana Ofotokoza Zinthu Zosiyana
Kachisi Amene Ezekieli Anaona M’masomphenya:
-
Anafotokozedwa ndi Ezekieli pofuna kuthandiza Ayuda amene anali ku ukapolo ku Babulo
-
Ali ndi guwa lansembe pamene pankaperekedwa nsembe zambiri
-
Akusonyeza mfundo zolungama zimene Yehova amafuna kuti tizitsatira pomulambira
-
Akutithandiza kumvetsa kubwezeretsa kwauzimu kumene kunayambika mu 1919
Kachisi Wamkulu Wauzimu:
-
Anafotokozedwa ndi Paulo m’kalata imene analembera Akhristu a Chiheberi
-
Ali ndi guwa lansembe pamene panaperekedwa nsembe imodzi “kamodzi kokha” (Aheb. 10:10)
-
Akufotokoza za kulambira Yehova m’njira yovomerezeka kudzera mu nsembe ya dipo ya Khristu zomwe zinkaimiliridwa ndi chihema komanso akachisi
-
Amatithandiza kumvetsa ntchito imene Khristu anagwira monga Mkulu wa Ansembe wamkulu kuchokera mu 29 mpaka 33 C.E.