Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

Pitani ku mitu ya nkhani

BOKOSI 16B

Kuusa Moyo ndi Kubuula, Kulemba Chizindikiro Komanso Kuphwanya—Kodi Zimenezi Zidzachitika Liti Nanga Zidzachitika Bwanji?

Kuusa Moyo ndi Kubuula, Kulemba Chizindikiro Komanso Kuphwanya—Kodi Zimenezi Zidzachitika Liti Nanga Zidzachitika Bwanji?

Masomphenya amene ali mu Ezekieli chaputala 9 akukwaniritsidwanso masiku ano. Tikamvetsa mmene zinthu zidzakhalire, zingatithandize kukhala olimba mtima pamene mapeto a dziko loipali akuyandikira

“Kuusa moyo ndi kubuula”

KODI KUDZACHITIKA LITI?: M’masiku otsiriza chisautso chachikulu chisanayambe

KODI KUDZACHITIKA BWANJI?: Anthu owongoka mtima akusonyeza mwa zolankhula ndi zochita zawo kuti akudana ndi makhalidwe oipa a m’dzikoli. Anthu amenewa amamvetsera uthenga wabwino umene ukulalikidwa, akupitiriza kusonyeza makhalidwe a Khristu, amabatizidwa posonyeza kuti anadzipereka kwa Yehova ndipo amathandiza mokhulupirika abale ake a Khristu

“Kulemba chizindikiro”

KODI KUDZACHITIKA LITI?: Pa chisautso chachikulu

KODI KUDZACHITIKA BWANJI?: Munthu amene ali ndi kachikwama ka mlembi konyamuliramo inki akuimira Yesu Khristu akadzabwera ngati woweruza wa mitundu yonse ya anthu. A khamu lalikulu adzaweruzidwa kapena kuti kulembedwa chizindikiro kuti ndi nkhosa. Zimenezi zikusonyeza kuti adzapulumuka pa Aramagedo

“Kuphwanya”

KODI KUDZACHITIKA LITI?: Pa Aramagedo

KODI KUDZACHITIKA BWANJI?: Yesu Khristu ndi gulu lake lankhondo lakumwamba, lomwe ndi angelo komanso olamulira anzake okwana 144,000, adzawonongeratu dziko loipali n’kupulumutsa anthu amene akulambira Mulungu woona ndipo adzawalowetsa dziko lapansi latsopano lolungama