Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

Pitani ku mitu ya nkhani

BOKOSI 9D

Maulosi Okhudza Ukapolo ndi Kubwezeretsedwa

Maulosi Okhudza Ukapolo ndi Kubwezeretsedwa

Maulosi ambiri okhudza ukapolo wa Ayuda ku Babulo wakale anakwaniritsidwa m’njira ziwiri. Kukwaniritsidwa kwakukulu kunachitika pamene Akhristu anatengedwa kupita ku ukapolo ku Babulo Wamkulu. Onani zitsanzo zotsatirazi.

1. MACHENJEZO

2. UKAPOLO

3. KUBWEZERETSEDWA

KUKWANIRITSIDWA KOYAMBA

Chaka cha 607 B.C.E. chisanafike​—Yesaya, Yeremiya ndi Ezekieli anachenjeza anthu a Mulungu koma anthu ambiri anapitiriza kupandukira Mulungu

607 B.C.E.​—Yerusalemu anawonongedwa, anthu a Mulungu anatengedwa kupita ku ukapolo ku Babulo

537 B.C.E. kupita m’tsogolo​—Ayuda okhulupirika amene anatsala anabwerera ku Yerusalemu, anamanga kachisi n’kuyambiranso kulambira koyera

KUKWANIRITSIDWA KWAKUKULU

Nthawi ya atumwi​—Yesu, Paulo ndi Yohane anachenjeza mpingo komabe anthu anapitiriza kupandukira Mulungu

Kuyambira zaka za m’ma 100 C.E.​—Akhristu oona anatengedwa kupita ku ukapolo ku Babulo Wamkulu

1919 C.E. kupita m’tsogolo​—Yesu atayamba kulamulira monga mfumu, Akhristu okhulupirika odzozedwa anamasulidwa ku ukapolo wauzimu ndipo kulambira koyera kunabwezeretsedwa