BOKOSI 7A
Mitundu Imene Inazungulira Yerusalemu
cha m’ma 650-300 B.C.E.
TCHATI CHOSONYEZA NTHAWI (ZAKA ZONSE NDI ZA MU B.C.E.)
-
620: Ababulo anayamba kulamulira Yerusalemu
Nebukadinezara anachititsa kuti mfumu ya ku Yerusalemu ikhale pansi pa ulamuliro wake
-
617: Ababulo anatenga gulu loyamba la akapolo kuchokera ku Yerusalemu
Anatenga olamulira, asilikali amphamvu ndi amisiri n’kupita nawo ku Babulo
-
607: Ababulo anawononga Yerusalemu
Mzindawo ndi kachisi wake zinawotchedwa
-
Pambuyo pa 607: Mzinda wa Turo wakumtunda
Nebukadinezara anaukira mzinda wa Turo kwa zaka 13. Iye anagonjetsa mzinda wa Turo wakumtunda koma mzinda wa Turo wapachilumba anausiya
-
602: Aamoni ndi Amowabu
Nebukadinezara anaukira Aamoni ndi Amowabu
-
588: Ababulo anagonjetsa Aiguputo
M’chaka cha 37 cha ulamuliro wake, Nebukadinezara anaukira Aiguputo
-
332: Mzinda wa Turo wapachilumba
Gulu lankhondo la Agiriki limene ankalitsogolera ndi Alekizanda Wamkulu, linawononga mzinda wa Turo wapachilumba
-
332 kapena chakachi chisanafike: Filisitiya
Alekizanda anagonjetsa mzinda wa Gaza umene unali likulu la Afilisiti
Malo amene ali pa Mapu
-
GIRISI
-
NYANJA YAIKULU
-
(NYANJA YA MEDITERRANEAN)
-
TURO
-
Sidoni
-
Turo
-
Samariya
-
Yerusalemu
-
Gaza
-
FILISITIYA
-
IGUPUTO
-
BABULO
-
AMONI
-
MOWABU
-
EDOMU