PHUNZIRO 11
Kulankhula ndi Mtima Wonse
Aroma 12:11
MFUNDO YAIKULU: Muzilankhula ndi mtima wonse kuti muziwafika pamtima anthu amene mukukambirana nawo.
MMENE MUNGACHITIRE:
-
Muzilankhula kuchokera mumtima. Mukamakonzekera komanso kukamba nkhani, muziganizira mmene ingathandizire anthu. Muziidziwa bwino nkhaniyo moti muzilankhula mfundo zanu kuchokera mumtima.
-
Muziganizira anthu. Muziganizira mmene mfundo imene mungawerenge kapena kuphunzitsa ingathandizire anthu. Muzifotokoza mfundozo m’njira yoti anthu aziona kuti ndi zothandiza.
-
Nkhani yanu izikhala yamoyo. Muzisonyeza kuti nkhaniyo yakufikani pamtima. Ndiyeno manja ndi nkhope yanu zizisonyeza mmene mukumvera mumtima.