PHUNZIRO 12
Kulankhula Mwachikondi Komanso Mokoma Mtima
1 Atesalonika 2:7, 8
MFUNDO YAIKULU: Mukamalankhula, anthu aziona kuti mumawaganizira komanso mumawafunira zabwino.
MMENE MUNGACHITIRE:
-
Muziganizira anthu. Pokonzekera nkhani yanu muziganizira mavuto amene anthu akukumana nawo. Muziganiziranso mmene anthuwo akumvera chifukwa cha mavuto awo.
-
Muzisankha bwino mawu. Cholinga chanu chizikhala kuwalimbikitsa, kuwatonthoza komanso kuwapatsa mphamvu. Pewani kukhumudwitsa anthu, kudzudzula anthu omwe si Mboni kapena kutsutsa kwambiri mfundo zimene anthu ena amazikhulupirira kwambiri.
-
Muzisonyeza kuti mumakonda anthu. Mawu komanso nkhope yanu zizisonyeza kuti mumaganizira anthu. Muzikondanso kumwetulira.