PHUNZIRO 16
Kulankhula Molimbikitsa
Yobu 16:5
MFUNDO YAIKULU: M’malo mongotchula mavuto okhaokha, muzifotokoza njira yothetsera mavutowo komanso mfundo zimene zingalimbikitse anthu.
MMENE MUNGACHITIRE:
-
Muziona kuti anthu amene mukulankhula nawo ali ndi mtima wabwino. Muziona kuti Akhristu anzanu amafuna kusangalatsa Yehova. Ngakhale pamene mukufuna kuwapatsa malangizo, muziyamba ndi kuwayamikira kuchokera pansi pa mtima.
-
Chepetsani mfundo zosalimbikitsa. Zinthu zina zosalimbikitsa mukhoza kuzitchula ngati mukufuna kutsimikizira mfundo inayake. Koma nkhani yanu yonse iyenera kukhala yolimbikitsa.
-
Muzigwiritsa ntchito bwino Mawu a Mulungu. Thandizani anthu kuganizira zimene Yehova wachita m’mbuyomu, zimene akuchita panopa, ndiponso zimene adzachite m’tsogolo. Thandizani anthu kukhala ndi chiyembekezo komanso kuti alimbe mtima.