PHUNZIRO 19
Kuwafika Pamtima Anthu
MMENE MUNGACHITIRE:
-
Muzithandiza anthu kuti azidzifufuza. Muzifunsa mafunso othandiza anthu kudzifufuza mumtima.
-
Muzithandiza anthu kukhala ndi zolinga zabwino. Thandizani anthu kudzifufuza kuti adziwe chifukwa chimene amachitira zinthu zabwino. Athandizeni kuti azichita zinthu chifukwa chokonda Yehova, anzawo komanso Mawu a Mulungu. Muzikambirana ndi anthu osati kuwauza zochita. Nkhani yanu ikamatha, anthu azikhala atalimbikitsidwa osati atachititsidwa manyazi. Azifunitsitsa kuchita zonse zimene angathe.
-
Muzithandiza anthu kuganizira za Yehova. Nkhani yanu izithandiza anthu kuona kuti malamulo komanso mfundo za m’Baibulo zimasonyeza makhalidwe a Yehova monga chikondi. Muzithandiza anthu kudziwa kuti zochita zawo zimakhudza Yehova ndipo azifunitsitsa kumusangalatsa.