PHUNZIRO 5
Kuwerenga Molondola
MMENE MUNGACHITIRE:
-
Muzikonzekera bwino. Muzidzifunsa kuti, N’chifukwa chiyani mawu amenewa analembedwa? Muziwerenga magulu a mawu osati kumangotchula liwu ndi liwu. Muzipewa kuwonjezera mawu, kudumpha mawu kapena kusemphanitsa mawu. Muzitsatira zizindikiro zonse za m’kalembedwe.
-
Muzitchula mawu alionse molondola. Ngati simukudziwa katchulidwe kabwino ka mawu, muyenera kufufuza, kumvetsera nkhani zojambulidwa kapena kufunsa anzanu omwe amadziwa bwino.
-
Muzilankhula momveka bwino. Kuti mawu anu azituluka bwino muyenera kukweza bwino mutu komanso kutsegula pakamwa mokwanira. Muzitchula mawu alionse momveka bwino.